< Psalms 58 >

1 `In Ebreu thus, To victorie; `lese thou not the swete song, ether the semely salm, of Dauid. `In Jeroms translacioun thus, To the ouercomere, that thou lese not Dauid, meke and simple. Forsothe if ye speken riytfulnesse verili; ye sones of men, deme riytfuli.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 For in herte ye worchen wickidnesse in erthe; youre hondis maken redi vnriytfulnessis.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Synneris weren maad aliens fro the wombe; thei erriden fro the wombe, thei spaken false thingis.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Woodnesse is to hem, bi the licnesse of a serpent; as of a deef snake, and stoppynge hise eeris.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Which schal not here the vois of charmeris; and of a venym makere charmynge wiseli.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 God schal al to-breke the teeth of hem in her mouth; the Lord schal breke togidere the greet teeth of liouns.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Thei schulen come to nouyt, as water rennynge awei; he bente his bouwe, til thei ben maad sijk.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 As wexe that fletith awei, thei schulen be takun awei; fier felle aboue, and thei siyen not the sunne.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Bifore that youre thornes vndurstoden the ramne; he swolewith hem so in ire, as lyuynge men.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 The iust man schal be glad, whanne he schal se veniaunce; he schal waische hise hondis in the blood of a synner.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 And a man schal seie treuli, For fruyt is to a iust man; treuli God is demynge hem in erthe.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Psalms 58 >