< Psalms 53 >

1 To the ouercomer bi the quere, the lernyng of Dauid. The vnwise man seide in his herte; God is not. Thei ben `corrupt, and maad abhomynable in her wickidnessis; noon is that doith good.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 God bihelde fro heuene on the sones of men; that he se, if `ony is vndurstondynge, ether sekynge God.
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Alle boweden awei, thei ben maad vnprofitable togidre; noon is that doith good, ther is not til to oon.
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 Whether alle men, that worchen wickidnesse, schulen not wite; whiche deuouren my puple as the mete of breed?
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Thei clepiden not God; there thei trembliden for drede, where no drede was. For God hath scaterid the boones of hem, that plesen men; thei ben schent, for God hath forsake hem.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Who schal yyue fro Syon helthe to Israel? whanne the Lord hath turned the caitifte of his puple, Jacob schal `ful out make ioie, and Israel schal be glad.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

< Psalms 53 >