< Psalms 49 >

1 To victorie, a salm to the sones of Chore. Alle ye folkis, here these thingis; alle ye that dwellen in the world, perseyue with eeris.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Alle the sones of erthe and the sones of men; togidere the riche man and the pore in to oon.
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 Mi mouth schal speke wisdom; and the thenkyng of myn herte schal speke prudence.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 I schal bouwe doun myn eere in to a parable; Y schal opene my resoun set forth in a sautree.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Whi schal Y drede in the yuel dai? the wickidnesse of myn heele schal cumpasse me.
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 Whiche tristen in her owne vertu; and han glorie in the multitude of her richessis.
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 A brother ayenbieth not, schal a man ayenbie? and he schal not yyue to God his plesyng.
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 And he schal not yyue the prijs of raunsum of his soule; and he schal trauele with outen ende,
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 and he schal lyue yit in to the ende.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 He schal not se perischyng, whanne he schal se wise men diynge; the vnwise man and fool schulen perische togidere. And thei schulen leeue her richessis to aliens;
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 and the sepulcris of hem ben the housis of hem with outen ende. The tabernaclis of hem ben in generacioun and generacioun; thei clepiden her names in her londis.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 A man, whanne he was in honour, vndurstood not; he is comparisound to vnwise beestis, and he is maad lijk to tho.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 This weie of hem is sclaundir to hem; and aftirward thei schulen plese togidere in her mouth.
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 As scheep thei ben set in helle; deth schal gnawe hem. And iust men schulen be lordis of hem in the morewtid; and the helpe of hem schal wexe eld in helle, for the glorie of hem. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 Netheles God schal ayenbie my soule from the power of helle; whanne he schal take me. (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Drede thou not, whanne a man is maad riche; and the glorie of his hows is multiplied.
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 For whanne he schal die, he schal not take alle thingis; and his glorie schal not go doun with him.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 For his soule schal be blessid in his lijf; he schal knouleche to thee, whanne thou hast do wel to hym.
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 He schal entre til in to the generaciouns of hise fadris; and til in to with outen ende he schal not se liyt.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 A man, whanne he was in honour, vndurstood not; he is comparisound to vnwise beestis, and is maad lijk to tho.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Psalms 49 >