< Psalms 32 >

1 Lernyng to Dauid. Blessid ben thei, whose wickidnessis ben foryouun; and whose synnes ben hilid.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Blessid is the man, to whom the Lord arrettide not synne; nethir gile is in his spirit.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 For Y was stille, my boonys wexiden elde; while Y criede al dai.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 For bi dai and nyyt thin `hond was maad greuouse on me; Y am turned in my wretchednesse, while the thorn is set in.
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 I made my synne knowun to thee; and Y hidde not my vnriytfulnesse. I seide, Y schal knouleche ayens me myn vnriytfulnesse to the Lord; and thou hast foryoue the wickidnesse of my synne.
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 For this thing ech hooli man schal preye to thee; in couenable tyme. Netheles in the greet flood of many watris; tho schulen not neiye to thee.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Thou art my refuyt fro tribulacioun, that cumpasside me; thou, my fulli ioiyng, delyuere me fro hem that cumpassen me.
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Y schal yyue vnderstondyng to thee, and Y schal teche thee; in this weie in which thou schalt go, Y schal make stidefast myn iyen on thee.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Nile ye be maad as an hors and mule; to whiche is noon vndurstondyng. Lord, constreyne thou the chekis of hem with a bernacle and bridil; that neiyen not to thee.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Many betyngis ben of the synnere; but merci schal cumpasse hym that hopith in the Lord.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Ye iust men, be glad, and make fulli ioie in the Lord; and alle ye riytful of herte, haue glorie.
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Psalms 32 >