< Psalms 22 >

1 To ouercome, for `the morewtid hynd; the salm of Dauid. God, my God, biholde thou on me, whi hast thou forsake me? the wordis of my trespassis ben fer fro myn helthe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 Mi God, Y schal crye bi dai, and thou schalt not here; and bi nyyt, and not to vnwisdom to me.
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 Forsothe thou, the preisyng of Israel, dwellist in holynesse;
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 oure fadris hopiden in thee, thei hopiden, and thou delyueridist hem.
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 Thei crieden to thee, and thei weren maad saaf; thei hopiden in thee, and thei weren not schent.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 But Y am a worm, and not man; the schenschip of men, and the outcastyng of the puple.
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 Alle men seynge me scorneden me; thei spaken with lippis, and stiriden the heed.
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 He hopide in the Lord, delyuere he hym; make he hym saaf, for he wole hym.
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 For thou it art that drowist me out of the wombe, thou art myn hope fro the tetis of my modir;
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 in to thee Y am cast forth fro the wombe. Fro the wombe of my modir thou art my God; departe thou not fro me.
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 For tribulacioun is next; for noon is that helpith.
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Many calues cumpassiden me; fatte bolis bisegiden me.
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Thei openyden her mouth on me; as doith a lioun rauyschynge and rorynge.
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 I am sched out as watir; and alle my boonys ben scaterid. Myn herte is maad, as wex fletynge abrood; in the myddis of my wombe.
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Mi vertu driede as a tiyl stoon, and my tunge cleuede to my chekis; and thou hast brouyt forth me in to the dust of deth.
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 For many doggis cumpassiden me; the counsel of wickid men bisegide me. Thei delueden myn hondis and my feet;
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 thei noumbriden alle my boonys. Sotheli thei lokiden, and bihelden me;
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 thei departiden my clothis to hem silf, and thei senten lot on my cloth.
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 But thou, Lord, delaie not thin help fro me; biholde thou to my defence.
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 God, delyuere thou my lijf fro swerd; and delyuere thou myn oon aloone fro the hond of the dogge.
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Make thou me saaf fro the mouth of a lioun; and my mekenesse fro the hornes of vnycornes.
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 I schal telle thi name to my britheren; Y schal preise thee in the myddis of the chirche.
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 Ye that dreden the Lord, herie hym; alle the seed of Jacob, glorifie ye hym.
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 Al the seed of Israel drede hym; for he forsook not, nethir dispiside the preier of a pore man. Nethir he turnede awei his face fro me; and whanne Y criede to hym, he herde me.
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 Mi preisyng is at thee in a greet chirche; Y schal yelde my vowis in the siyt of men dredynge hym.
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 Pore men schulen ete, and schulen be fillid, and thei schulen herie the Lord, that seken hym; the hertis of hem schulen lyue in to the world of world.
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 Alle the endis of erthe schulen bithenke; and schulen be conuertid to the Lord. And alle the meynees of hethene men; schulen worschipe in his siyt.
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 For the rewme is the Lordis; and he schal be Lord of hethene men.
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 Alle the fatte men of erthe eeten and worschipiden; alle men, that goen doun in to erthe, schulen falle doun in his siyt.
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 And my soule schal lyue to hym; and my seed schal serue him.
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 A generacioun to comyng schal be teld to the Lord; and heuenes schulen telle his riytfulnesse to the puple that schal be borun, whom the Lord made.
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.

< Psalms 22 >