< Proverbs 26 >

1 As snow in somer, and reyn in heruest; so glorie is vnsemeli to a fool.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 For whi as a brid fliynge ouer to hiy thingis, and a sparowe goynge in to vncerteyn; so cursing brouyt forth with out resonable cause schal come aboue in to sum man.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Beting to an hors, and a bernacle to an asse; and a yerde in the bak of vnprudent men.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Answere thou not to a fool bi his foli, lest thou be maad lijk hym.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Answere thou a fool bi his fooli, lest he seme to him silf to be wijs.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 An haltinge man in feet, and drinkinge wickidnesse, he that sendith wordis by a fonned messanger.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 As an haltinge man hath faire leggis in veyn; so a parable is vnsemeli in the mouth of foolis.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 As he that casteth a stoon in to an heep of mercurie; so he that yyueth onour to an vnwijs man.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 As if a thorn growith in the hond of a drunkun man; so a parable in the mouth of foolis.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Doom determyneth causis; and he that settith silence to a fool, swagith iris.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 As a dogge that turneth ayen to his spuyng; so is an vnprudent man, that rehersith his fooli.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Thou hast seyn a man seme wijs to hym silf; an vnkunnyng man schal haue hope more than he.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 A slow man seith, A lioun is in the weie, a liounnesse is in the foot pathis.
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 As a dore is turned in his hengis; so a slow man in his bed.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 A slow man hidith hise hondis vndur his armpit; and he trauelith, if he turneth tho to his mouth.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 A slow man semeth wysere to hym silf, than seuene men spekynge sentensis.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 As he that takith a dogge bi the eeris; so he that passith, and is vnpacient, and is meddlid with the chiding of anothir man.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 As he is gilti, that sendith speris and arowis in to deth;
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 so a man that anoieth gilefuli his frend, and whanne he is takun, he schal seie, Y dide pleiynge.
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Whanne trees failen, the fier schal be quenchid; and whanne a priuy bacbitere is withdrawun, stryues resten.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 As deed coolis at quic coolis, and trees at the fier; so a wrathful man reisith chidyngis.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 The wordis of a pryuei bacbitere ben as symple; and tho comen til to the ynneste thingis of the herte.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 As if thou wolt ourne a vessel of erthe with foul siluer; so ben bolnynge lippis felouschipid with `the werste herte.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 An enemy is vndirstondun bi hise lippis, whanne he tretith giles in the herte.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Whanne he `makith low his vois, bileue thou not to hym; for seuene wickidnessis ben in his herte.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 The malice of hym that hilith hatrede gilefuli, schal be schewid in a counsel.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 He that delueth a diche, schal falle in to it; and if a man walewith a stoon, it schal turne ayen to hym.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 A fals tunge loueth not treuth; and a slidir mouth worchith fallyngis.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbs 26 >