< Proverbs 23 >

1 Whanne thou sittist, to ete with the prince, perseyue thou diligentli what thingis ben set bifore thi face,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 and sette thou a withholding in thi throte. If netheles thou hast power on thi soule,
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 desire thou not of his metis, in whom is the breed of `a leesing.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Nyle thou trauele to be maad riche, but sette thou mesure to thi prudence.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Reise not thin iyen to richessis, whiche thou maist not haue; for tho schulen make to hem silf pennes, as of an egle, and tho schulen flee in to heuene.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Ete thou not with an enuyouse man, and desire thou not hise metis;
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 for at the licnesse of a fals dyuynour and of a coniectere, he gessith that, that he knowith not. He schal seie to thee, Ete thou and drinke; and his soule is not with thee.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Thou schalt brake out the metis, whiche thou hast ete; and thou schalt leese thi faire wordis.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Speke thou not in the eeris of vnwise men; for thei schulen dispise the teching of thi speche.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Touche thou not the termes of litle children; and entre thou not in to the feeld of fadirles and modirles children.
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 For the neiybore of hem is strong, and he schal deme her cause ayens thee.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Thin herte entre to techyng, and thin eeris `be redi to the wordis of kunnyng.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Nile thou withdrawe chastisyng fro a child; for thouy thou smyte hym with a yerde, he schal not die.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Thou schalt smyte hym with a yerde, and thou schalt delyuere his soule fro helle. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Mi sone, if thi soule is wijs, myn herte schal haue ioye with thee;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 and my reynes schulen make ful out ioye, whanne thi lippis speken riytful thing.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Thin herte sue not synneris; but be thou in the drede of the Lord al dai.
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 For thou schalt haue hope at the laste, and thin abidyng schal not be don awei.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Mi sone, here thou, and be thou wijs, and dresse thi soule in the weie.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Nyle thou be in the feestis of drinkeris, nether in the ofte etyngis of hem, that bryngen togidere fleischis to ete.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For men yyuynge tent to drinkis, and yyuyng mussels togidere, schulen be waastid, and napping schal be clothid with clothis.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Here thi fadir, that gendride thee; and dispise not thi modir, whanne sche is eld.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Bie thou treuthe, and nyle thou sille wisdom, and doctryn, and vndurstonding.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 The fadir of a iust man ioieth ful out with ioie; he that gendride a wijs man, schal be glad in hym.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Thi fadir and thi modir haue ioye, and he that gendride thee, make ful out ioye.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 My sone, yyue thin herte to me, and thin iyen kepe my weyes.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 For an hoore is a deep diche, and an alien womman is a streit pit.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Sche settith aspie in the weie, as a theef; and sche schal sle hem, whiche sche schal se vnwar.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 To whom is wo? to whos fadir is wo? to whom ben chidingis? to whom ben dichis? to whom ben woundis with out cause? to whom is puttyng out of iyen?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Whether not to hem, that dwellen in wyn, and studien to drynke al of cuppis?
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Biholde thou not wyn, whanne it sparclith, whanne the colour therof schyneth in a ver.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 It entrith swetli, but at the laste it schal bite as an eddre doith, and as a cocatrice it schal schede abrood venyms.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Thin iyen schulen se straunge wymmen, and thi herte schal speke weiwerd thingis.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 And thou schalt be as a man slepinge in the myddis of the see, and as a gouernour aslepid, whanne the steere is lost.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 And thou schalt seie, Thei beeten me, but Y hadde not sorewe; thei drowen me, and Y feelide not; whanne schal Y wake out, and Y schal fynde wynes eft?
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbs 23 >