< Proverbs 17 >

1 Betere is a drie mussel with ioye, than an hous ful of sacrifices with chidyng.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 A wijs seruaunt schal be lord of fonned sones; and he schal departe eritage among britheren.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 As siluer is preued bi fier, and gold is preued bi a chymnei, so the Lord preueth hertis.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 An yuel man obeieth to a wickid tunge; and a fals man obeieth to false lippis.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 He that dispisith a pore man, repreueth his maker; and he that is glad in the fallyng of another man, schal not be vnpunyschid.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 The coroun of elde men is the sones of sones; and the glorie of sones is the fadris of hem.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Wordis wel set togidere bisemen not a fool; and a liynge lippe bicometh not a prince.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 A preciouse stoon moost acceptable is the abiding of hym that sekith; whidur euere he turneth hym silf, he vndurstondith prudentli.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 He that helith trespas, sekith frenschipis; he that rehersith bi an hiy word, departith hem, that ben knyt togidere in pees.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 A blamyng profitith more at a prudent man, than an hundryd woundis at a fool.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Euere an yuel man sekith stryues; forsothe a cruel aungel schal be sent ayens hym.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 It spedith more to meete a femal bere, whanne the whelpis ben rauyschid, than a fool tristynge to hym silf in his foli.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Yuel schal not go a wei fro the hous of hym, that yeldith yuels for goodis.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 He that leeueth watir, is heed of stryues; and bifor that he suffrith wrong, he forsakith dom.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 Bothe he that iustifieth a wickid man, and he that condempneth a iust man, euer ethir is abhomynable at God.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 What profitith it to a fool to haue richessis, sithen he mai not bie wisdom? He that makith his hous hiy, sekith falling; and he that eschewith to lerne, schal falle in to yuels.
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 He that is a frend, loueth in al tyme; and a brother is preuyd in angwischis.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 A fonned man schal make ioie with hondis, whanne he hath bihiyt for his frend.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 He that bithenkith discordis, loueth chidingis; and he that enhaunsith his mouth, sekith fallyng.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 He that is of weiward herte, schal not fynde good; and he that turneth the tunge, schal falle in to yuel.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 A fool is borun in his schenschipe; but nether the fadir schal be glad in a fool.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 A ioiful soule makith likinge age; a sorewful spirit makith drie boonys.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 A wickid man takith yiftis fro the bosum, to mys turne the pathis of doom.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Wisdom schyneth in the face of a prudent man; the iyen of foolis ben in the endis of erthe.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 A fonned sone is the ire of the fadir, and the sorewe of the modir that gendride hym.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 It is not good to brynge in harm to a iust man; nether to smyte the prince that demeth riytfuli.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 He that mesurith his wordis, is wijs and prudent; and a lerud man is of preciouse spirit.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Also a foole, if he is stille, schal be gessid a wijs man; and, if he pressith togidre hise lippis, he `schal be gessid an vndurstondynge man.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Proverbs 17 >