< Proverbs 10 >

1 The parablis of Salomon. A wijs sone makith glad the fadir; but a fonned sone is the sorewe of his modir.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Tresouris of wickidnesse schulen not profite; but riytfulnesse schal delyuere fro deth.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 The Lord schal not turmente the soule of a iust man with hungur; and he schal distrie the tresouns of vnpitouse men.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 A slow hond hath wrouyt nedynesse; but the hond of stronge men makith redi richessis. Forsothe he that enforsith to gete `ony thing bi leesyngis, fedith the wyndis; sotheli the same man sueth briddis fleynge.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 He that gaderith togidere in heruest, is a wijs sone; but he that slepith in sommer, is a sone of confusioun.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 The blessing of God is ouer the heed of a iust man; but wickidnesse hilith the mouth of wickid men.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 The mynde of a iust man schal be with preisingis; and the name of wickid men schal wexe rotun.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 A wijs man schal resseyue comaundementis with herte; a fool is betun with lippis.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 He that goith simpli, goith tristili; but he that makith schrewid hise weies, schal be opyn.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 He that bekeneth with the iye, schal yyue sorewe; a fool schal be betun with lippis.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 The veyne of lijf is the mouth of a iust man; but the mouth of wickid men hilith wickidnesse.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Hatrede reisith chidingis; and charite hilith alle synnes.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Wisdom is foundun in the lippis of a wise man; and a yerd in the bak of him that is nedi of herte.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Wise men hiden kunnyng; but the mouth of a fool is nexte to confusioun.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 The catel of a riche man is the citee of his strengthe; the drede of pore men is the nedynesse of hem.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 The werk of a iust man is to lijf; but the fruyt of a wickid man is to synne.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 The weie of lijf is to him that kepith chastising; but he that forsakith blamyngis, errith.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 False lippis hiden hatrede; he that bringith forth dispisinge is vnwijs.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Synne schal not faile in myche spekyng; but he that mesurith hise lippis, is moost prudent.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Chosun siluer is the tunge of a iust man; the herte of wickid men is for nouyt.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 The lippis of a iust man techen ful manye men; but thei that ben vnlerned, schulen die in nedinesse of herte.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 The blessing of the Lord makith riche men; and turment schal not be felowschipid to hem.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 A fool worchith wickidnesse as bi leiyyng; but `wisdom is prudence to a man.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 That that a wickid man dredith, schal come on hym; the desire of iust men schalbe youun to hem.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 As a tempeste passynge, a wickid man schal not be; but a iust man schal be as an euerlastynge foundement.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 As vynegre noieth the teeth, and smoke noieth the iyen; so a slow man noieth hem that senten hym in the weie.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 The drede of the Lord encreesith daies; and the yeeris of wickid men schulen be maad schort.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Abiding of iust men is gladnesse; but the hope of wickid men schal perische.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 The strengthe of a symple man is the weie of the Lord; and drede to hem that worchen yuel.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 A iust man schal not be moued with outen ende; but wickid men schulen not dwelle on the erthe.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 The mouth of a iust man schal bringe forth wisdom; the tunge of schrewis schal perische.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 The lippis of a iust man biholden pleasaunt thingis; and the mouth of wickid men byholdith weiward thingis.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Proverbs 10 >