< Numbers 27 >

1 Forsothe the douytris of Salphaat, sone of Epher, sone of Galaad, sone of Machir, sone of Manasses, that was `the sone of Joseph, neiyeden; of whiche douytris these ben the names; Maala, and Noha, and Egla, and Melcha, and Thersa.
Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
2 And thei stoden bifore Moises, and Eleazar, preest, and alle the princes of the puple, at the dore of tabernacle of boond of pees; and seiden,
pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
3 Oure fadir was deed in the deseert, nether he was in the rebelte, that was reisid ayens the Lord, vndur Chore, but he was deed in his synne; he hadde no male sones. Whi is `the name of hym takun awei fro his meynee, for he hath no sone? Yif ye possessioun to vs among `the kynesmen of oure fadir.
“Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
4 And Moises telde `the cause of hem to the doom of the Lord;
Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
5 which seide to Moyses, The douytris of Salphaath axen a iust thing; yyue thou possessioun to hem among `the kynnysmen of her fadir,
Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
6 and be thei successouris to hym in to eritage.
ndipo Yehova anati kwa iye,
7 Forsothe thou schalt speke these thingis to the sons of Israel,
“Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
8 Whanne a man is deed with out sone, the eritage schal go to his douyter;
“Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
9 if he hath not a douyter, he schal haue eiris his britheren;
Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
10 that and if britheren ben not, ye schulen yyue the eritage to `the britheren of his fadir;
Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
11 forsothe if he hath no britheren of his fadir, the eritage schal be youun to hem that ben next to hym. And this schal be hooli, `that is, stidefast, bi euerlastynge lawe to the sones of Israel, as the Lord comaundide to Moises.
Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
12 Also the Lord seide to Moises, Stie thou in to this hil of Aberym, and biholde thou fro thennus the lond, which Y schal yyue to the sones of Israel.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
13 And whanne thou hast seyn it, also thou schalt go to thi puple, as thi brother Aaron yede;
Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
14 for thou offenddidist me in the deseert of Syn, in the ayen seiyng of the multitude, nether woldist halewe me bifor it, on the watris. These ben the watris of ayen seiyng, in Cades, of the deseert of Syn.
chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
15 To whom Moises answeryde,
Mose anati kwa Yehova,
16 The Lord God of spiritis of al fleisch puruey a man, that be on this multitude,
“Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
17 and may go out, and entre bifor hem, and lede hem out, and lede hem yn, lest the `puple of the Lord be as scheep with out schepherde.
alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
18 And the Lord seide to hym, Take thou Josue, the sone of Nun, a man in whom the spyrit of God is, and set thin hond on hym; and he schal stonde bifore Eleazar,
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
19 preest, and bifore al the multitude.
Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
20 And thou schalt yyue to hym comaundementis, in the siyt of alle men, and a part of thi glorie, that al the synagoge of the sones of Israel here hym.
Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
21 If ony thing schal be worthi to be do for this man, Eleasar, preest, schal counseil the Lord; he schal go out, and schal go yn, at the word of Eleazar; he, and alle the sones of Israel with him, and the tother multitude.
Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
22 Moises dide as the Lord comaundide, and whanne he hadde take Josue, he settide hym bifore Eleazar, preest, and bifore al the multitude of the puple;
Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
23 and whanne he hadde set hondis on his heed, he reherside alle thingis whiche the Lord comaundide.
Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.

< Numbers 27 >