< Numbers 26 >

1 Aftir that the blood of gilti men was sched out, the Lord seide to Moises and to Eleasar,
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 preest, sone of Aaron, Noumbre ye al the summe of the sones of Israel, fro twenti yeer and aboue, bi her housis, and kynredis, alle men that mowen go forth to batels.
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 And so Moises and Eleasar, preest, spaken in the feeldi places of Moab, ouer Jordan, ayens Jerico, to hem that weren of twenti yeer and aboue,
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 as the Lord comaundide; of whiche this is the noumbre.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Ruben, the firste gendrid of Israel; the sone of hym was Enoch, of whom was the meynee of Enochitis; and Phallu, of whom the meynee of Phalluytis; and Esrom,
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 of whom the meynee of Esromytis; and Charmy, of whom the meynee of Charmytis.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 Thes weren the meynees of the generacioun of Ruben, of whiche meynees the noumbre was foundun thre and fourti thousand seuene hundrid and thretti.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 The sone of Phallu was Heliab;
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 the sones of hym weren Namuel, and Dathan and Abiron. `These weren Dathan and Abiron, prynces of the puple, that riseden ayens Moises and Aaron, in the rebelte of Chore, whanne thei rebelliden ayens the Lord;
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 and the erthe openyde his mouth, and deuouride Chore, while ful many men dieden, whanne the fier brente two hundrid men and fifti; and a greet myracle was maad,
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 that whanne Chore perischide, hise sones perischiden not.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 The sones of Symeon bi her kynredis; Namuel, of hym was the meynee of Namuelitis; Jamyn, of hym was the meynee of Jamynytis; Jachin, of hym was the meynee of Jachynytis;
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 Zare, of hym the meynee of Zarenytis; Saul, of hym the meynee of Saulitis.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 These weren the meynees of Symeon, of whiche all the noumbre was two and twenti thousynde and two hundrid.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 The sones of Gad bi her kynredis; Sephon, of hym the meynee of Sephonytis; Aggi, of hym the meynee of Aggitis; Sumy, of hym the meynee of Sumytis;
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 Ozny, of hym the meynee of Oznytis; Heri, of hym the meynee of Hereytis;
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 Arod, of hym the meynee of Aroditis; Ariel, of hym the meynee of Arielitis.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 These weren the meynees of Gad, of whiche al the noumbre was fourti thousynde and fyue hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 The sones of Juda weren Her and Onan, whiche bothe weren deed in the lond of Canaan.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 And the sones of Juda weren bi her kynredis; Sela, of whom the meynee of Selaitis; Phares, of whom the meynee of Pharesitis; Zare, of whom the meynee of Zareitis.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 Sotheli the sones of Phares weren Esrom, of whom the meynee of Esromytis; and Amul, of whom the meynee of Amulitis.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 These weren the meynees of Juda, of whiche al the noumbre was seuenty thousynde and fyue hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 The sones of Isachar bi her kynredis; Thola, of whom the meynee of Tholaitis; Phua, of whom the meynee of Phuitis;
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 Jasub, of whom the meynee of Jasubitis; Semran, of whom the meynee of Semranytis.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 These weren the kynredis of Isachar, of whiche the noumbre was foure and sixti thousynd and three hundrid.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 The sones of Zabulon bi her kinredis; Sarad, of whom the meynee of Sareditis; Helon, of whom the meynee of Helonytis; Jalel, of whom the meynee of Jalelitis.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 These weren the kynredis of Zabulon, of whiche the noumbre was sixti thousynde and fyue hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 The sones of Joseph bi her kynredis weren Manasses and Effraym.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 Of Manasses was borun Machir, of whom the meynee of Machiritis. Machir gendride Galaad, of whom the meynee of Galaditis.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 Galaad hadde sones; Hizezer, of whom the meynee of Hizezeritis; and Helech, of whom the meynee of Helechitis;
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 and Ariel, of whom the meynee of Arielitis; and Sechem, of whom the meynee of Sechemytis;
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 and Semyda, of whom the meynee of Semydaitis; and Epher, of whom the meynee of Epheritis.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 Forsothe Epher was the fadir of Salphath, that hadde not sones, but oneli douytris; of whiche these weren the names; Maala, and Noha, and Egla, and Melcha, and Thersa.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 These weren the meynees of Manasse, and the noumbre of hem was two and fifty thousynde and seuene hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 Forsothe the sones of Effraym bi her kynredis weren these; Suthala, of whom the meynee of Suthalaitis; Bether, of whom the meynee of Betherytis; Tehen, of whom the meynee of Thehenytis.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 Forsothe the sone of Suthala was Heram, of whom the meynee of Heramytis.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 These weren the kynredis `of the sones of Effraym, of whiche the noumbre was two and thretti thousynde and fyue hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 These weren the sones of Joseph, bi her meynees. The sones of Beniamyn in her kynredis; Bale, of whom the meynee of Baleytis; Azbel, of whom the meynee of Azbelitis; Ahiram, of whom the meynee of Ahiramitis;
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 Suphan, of whom the meynee of Suphanitis; Huphan, of whom the meynee of Huphanitis.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 The sones of Bale, Hered and Noeman; of Hered, the meyne of Hereditis; of Noeman, the meynee of Noemanitis.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 Thes weren the sones of Beniamyn bi her kynredis, of whiche the noumbre was fyue and fourti thousynde and sixe hundrid.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 The sones of Dan bi her kynredis; Suphan, of whom the meynee of Suphanytis. These weren the kynredis of Dan bi her meynees;
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 alle weren Suphanytis, of whiche the noumbre was foure and sixti thousynde and foure hundrid.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 The sones of Aser bi her kynredis; Jemma, of whom the meynee of Jemmaytis; Jesuy, of whom the meynee of Jesuytis; Brie, of whom the meynee of Brieitis.
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 The sones of Brie; Haber, of whom the meynee of Haberitis; and Melchiel, of whom the meynee of Melchielitis.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 Sotheli the name of `the douytir of Azer was Zara.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 These weren the kynredis of the sones of Aser, and the noumbre of hem was foure and fifti thousynde and foure hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 The sones of Neptalym bi her kynredis; Jesehel, of whom the meynee of Jeselitis; Guny, of whom the meynee of Gunytis;
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 Jeser, of whom the meynee of Jeserytis; Sellem, of whom the meynee of Sellemytis.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 Thes weren the kynredis of the sones of Neptalym bi her meynees, of whiche the noumbre was fyue and fourti thousynde and foure hundrid.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 This is the summe of the sones of Israel, that weren noumbrid, sixe hundrid thousynde and a thousynde seuene hundrid and thretti.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 And the Lord spak to Moises, and seide,
Yehova anawuza Mose kuti,
53 The lond schal be departid to these, bi the noumbre of names in to her possessiouns;
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 thou schalt yyue the grettere part to mo men, and the lesse part to fewere men; possessioun schal be youun to alle bi hem silf, as thei ben noumbrid now;
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 so oneli that lot departe the lond to lynagis and meynees.
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 What euer thing bifallith bi lot, ethir mo ether fewere men take this.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 Also this is the noumbre of the sones of Leuy bi her meynees; Gerson, of whom the meynee of Gersonytis; Caath, of whom the meynee of Caathitis; Merary, of whom the meynee of Meraritis.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 These weren the meynees of Leuy; the meynee of Lobny, the meynee of Ebron, the meynee of Mooli, the meynee of Musi, the meynee of Chori. And sotheli Caath gendride Amram,
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 which hadde a wijf, Jocabeth, douyter of Leuy, which douyter was borun to hym in Egipt. This Jocabeth gendride to hir hosebonde `Amram sones, Aaron, and Moyses, and Marie, `the sister of hem.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 Nadab, and Abyu, and Eleazar, and Ithamar weren bigetun of Aaron;
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 of whiche Nadab and Abyu weren deed, whanne thei hadden offrid alien fier bifor the Lord.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 And alle that weren noumbrid weren thre and twenti thousynde of male kynde, fro o monethe and aboue, whiche weren not noumbrid among the sones of Israel, nether possessioun was youun to hem with othir men.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 This is the noumbre of the sones of Israel, that weren discryued of Moises and Eleasar, preest, in the feeldi places of Moab, ouer Jordan, ayen Jerico;
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 among whiche noon of hem was that weren noumbrid bifor of Moises and Aaron, in the deseert of Synay;
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 for the Lord bifore seide, that alle schulden die in `the wildirnesse; and noon of hem dwellide, no but Caleph, `the sone of Jephone, and Josue, the sone of Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

< Numbers 26 >