< Nehemiah 6 >

1 Forsothe it was doon, whanne Sanaballath hadde herd, and Tobie, and Gosem of Arabie, and oure other enemyes, that Y hadde bildide the wal, and nomore brekyng was therynne; sotheli `til to that tyme Y hadde not set leeuys of schittyng in the yatis;
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 Sanaballath, and Tobie, and Gosem of Arabie senten to me, and seiden, Come thou, and smyte we boond of pees in calues, `in o feeld; forsothe thei thouyten for to do yuel to me.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 Therfor Y sente messangeris to hem, and Y seide, Y make a greet werk, and Y mai not go doun, lest perauenture it be doon retchelesli, whanne Y come, and go doun to you.
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 Sotheli thei senten to me `bi this word bi foure tymes, and Y answeride to hem by the formere word.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 And Sanaballath sente to me the fyuethe tyme bi the formere word his child; and he hadde in his hond a pistle writun in this maner;
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 It is herd among hethene men, and Gosem seide, that thou and the Jewis thenken for to rebelle, and therfor ye bilden, and thou wolt `reise thee king on hem;
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 for which cause also thou hast set profetis, that prechen of thee in Jerusalem, and seien, A king is in Jerusalem; the king schal here these wordis; therfor come thou now, that we take counsel togidere.
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 And Y sente to hem, and seide, It is not doon bi these wordis whiche thou spekist; for of thin herte thou makist these thingis.
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 Alle these men maden vs aferd, and thouyten that oure hondis schulden ceesse fro werkis, that we schulden reste; for which cause Y coumfortide more myn hond.
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 And Y entride priueli in to the hows of Samaie, sone of Dalie, the sone of Methabehel, which seide, Trete we with vs silf in the hows of God, in the myddis of the temple, and close we the yatis of the hows; for thei schulen come to sle thee, `and thei schulen come `bi niyt to sle thee.
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 And Y seide, Whether ony man lijk me fledde, and who as Y schal entre in to the temple, and schal lyue?
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 Y schal not entre. And Y vndurstood that God `hadde not sent hym, but `he spak as profesiynge to me; and Tobie and Sanaballath `hadden hirid hym for meede.
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 For he hadde take prijs, that Y schulde be aferd, and do, and that Y schulde do synne; and thei schulden haue yuel, which thei schulden putte to me with schenschip.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 Lord, haue mynde of me, for Tobye and Sanaballath, bi siche werkis `of hem; but also of Noadie, the profete, and of othere profetis, that maden me aferd.
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 Forsothe the wal was fillid in the fyue and twentithe dai of the monethe Ebul, in two and fifti daies.
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 Sotheli it was doon, whanne alle oure enemyes hadden herd, that alle hethene men dredden, that weren in oure cumpas, and thei felden doun with ynne hem silf, and wiste, that this work was maad of God.
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 But also in tho daies many pistlis of the principal men of Jewis weren sent to Tobie, and camen fro Tobie to hem.
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 For many men weren in Judee, and hadden his ooth; for he hadde weddid the douyter of Sechenye, the sone of Rotel; and Johannam, his sone, hadde take the douyter of Mosallam, sone of Barachie.
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 But also thei preisiden hym bifor me, and telden my wordis to hym; and Tobie sente lettris, for to make me aferd.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

< Nehemiah 6 >