< Micah 5 >

1 Now thou, douyter of a theef, schalt be distried; thei puttiden on vs bisegyng, in a yerde thei schulen smyte the cheke of the iuge of Israel.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 And thou, Bethleem Effrata, art litil in the thousyndis of Juda; he that is the lordli gouernour in Israel, schal go out of thee to me; and the goyng out of hym is fro bigynnyng, fro daies of euerlastyngnesse.
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 For this thing he shal yyue hem til to the tyme in which the trauelinge of child schal bere child, and the relifs of hise britheren schulen be conuertid to the sones of Israel.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 And he schal stonde, and schal fede in the strengthe of the Lord, in the heiythe of the name of his Lord God; and thei schulen be conuertid, for now he schal be magnefied til to the endis of al erthe.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 And this schal be pees, whanne Assirius schal come in to oure lond, and whanne he schal trede in oure housis; and we schulen reise on hym seuene scheepherdis, and eiyte primatis men, ether the firste in dignytee.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 And thei schulen frete the lond of Assur bi swerd, and the lond of Nembroth bi speris of hym; and he schal delyuere vs fro Assur, whanne he schal come in to oure lond, and whanne he schal trede in oure coostis.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 And relifs of Jacob schulen be in the myddil of many puplis, as dew of the Lord, and as dropis on erbe, whiche abidith not man, and schal not abide sones of men.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 And relifs of Jacob schulen be in hethene men, in the myddil of many puplis, as a lioun in beestis of the woodis, and as a whelpe of a lioun rorynge in flockis of scheep; and whanne he passith, and defoulith, and takith, there is not that schal delyuere.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 And thin hond schal be reisid on thin enemyes, and alle thin enemyes schulen perische.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 And it schal be, in that dai, seith the Lord, Y schal take awei thin horsis fro the myddil of thee, and Y schal distrie thi foure horsid cartis.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 And Y schal leese the citees of thi lond, and Y schal distrie alle thi strengthis;
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 and Y schal do awei witchecraftis fro thin hond, and dyuynaciouns schulen not be in thee.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 And Y schal make for to perische thi `grauun ymagis, and Y schal breke togidere fro the myddil of thee thin ymagis, and thou schalt no more worschipe the werkis of thin hondis.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 And Y schal drawe out of the middis of thee thi woodis, and Y schal al to-breke thi citees.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 And Y schal make in woodnesse and indignacioun veniaunce in alle folkis, whiche herden not.
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Micah 5 >