< Malachi 4 >

1 For lo! a dai schal come, brennynge as a chymenei; and alle proude men, and alle doynge vnpitee schulen be stobul; and the dai comynge schal enflaume hem, seith the Lord of oostis, which schal not leeue to hem rote and buriownyng.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi.
2 And to you dredynge my name the sunne of riytwisnesse schal rise, and heelthe in pennys of hym; and ye schulen go out, and schulen skippe, as a calf of the droue.
Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola.
3 And ye schulen to-trede vnpitouse men, whanne thei schulen be aische vndur the soole of youre feet, in the dai in which Y do, seith the Lord of oostis.
Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Bithenke ye on the lawe of my seruaunt Moises, which Y comaundide to hym in Oreb, to al Israel comaundementis and domes.
Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.
5 Lo! Y schal sende to you Elie, the profete, bifore that the greet dai and orible of the Lord come.
“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
6 And he schal conuerte the herte of fadris to sones, and the herte of sones to fadris of hem, lest perauenture Y come, and smyte the erthe with curs.
Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”

< Malachi 4 >