< Leviticus 27 >

1 And the Lord spak to Moises and seide, Speke thou to the sones of Israel,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 and thou schalt seye to hem, A man that makith avow, and bihetith his soule to God, schal yyue the priys vndur valu, ether preisyng.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
3 If it is a male, fro the twentithe yeer `til to the sixtithe yeer, he schal yyue fifti siclis of siluer, at the mesure of seyntuarie, if it is a womman,
mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
4 sche schal yyue thretti siclis;
Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
5 forsothe fro the fifthe yeer `til to the twentithe yeer, a male schal yyue twenti cyclis, a womman schal yyue ten ciclis;
Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
6 fro o monethe `til to the fifthe yeer, fyue ciclis schulen be youun for a male, thre ciclis for a womman;
Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
7 a male of sixti yeer and ouer schal yyue fiftene ciclis, a womman schal yyue ten cyclis.
Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
8 If it is a pore man, and may not yelde the valu, he schal stonde bifor the preest, and as myche as the preest preisith, and seeth that the pore man may yelde, so myche he schal yyue.
Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
9 Forsothe if ony man avowith a beeste, that may be offrid to the Lord, it schal be hooli,
“‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
10 and schal not mow be chaungid, that is, nethir a betere for `an yuel, nether `a worse for a good; and if he chaungith it, bothe that, that is chaungid, and that, for which it is chaungid, schal be halewid to the Lord.
Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
11 Sotheli if ony man avowith an vncleene beeste, that may not be offrid to the Lord, it schal be brouyt bifor the preest,
Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
12 and the preest schal deme whether it is good ether yuel, and schal sette the prijs;
ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
13 which prijs if he that offrith wole yyue, he schal adde the fifthe part ouer the valu.
Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
14 If a man avowith his hows, and halewith it to the Lord, the preest schal biholde, `whether it is good ether yuel, and bi the prijs, which is ordeyned of hym, it schal be seld;
“‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
15 sotheli if he that avowide wole ayen-bie it, he schal yyue the fifthe part of the valu aboue, and he schal haue the hows.
Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
16 That if he avowith the feeld of his possessioun, and halewith to the Lord, the prijs schal be demed bi the mesure of seed; if the feeld is sowun with thritti buyschels of barli, it schal be seeld for fifti siclys of siluer.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
17 If he auowith the feeld anoon for the yeer of the iubilee bigynnynge, as myche as it may be worth, bi so myche it schal be preisid;
Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
18 but if it be after `sum part of tyme, the preest schal rykene the money bi the noumbre of yeeris that ben residue `til to the iubilee, and it schal be withdrawun of the prijs.
Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
19 That if he that avowide wole ayenbie the feeld, he schal adde the fyuethe part of the money preisid, and he schal welde it;
Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
20 but if he nyle ayenbie, but it is seeld to ony othir man, he that avowide schal `no more mowe ayenbie it;
Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
21 for whanne the dai of iubilee cometh, it schal be halewid to the Lord, and the possessioun halewid perteyneth to the riyt of preestis.
Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
22 If the feeld is bouyt, and is not of the possessioun of grettere men,
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
23 and is halewid to the Lord, the preest schal determyne the prijs bi the noumbre of yeeris `til to the iubilee, and he that avowide the feeld schal yyue the prijs to the Lord;
wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
24 forsothe in the iubilee it schal turne ayen to the formere lord that seelde it, and `haue he in to the eritage of his possessioun.
Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
25 `Ech preisyng schal be peisid bi the sicle of seyntuarie; a sicle hath twenti halpens.
Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
26 No man may halewe and avowe the firste gendrid thingis that perteynen to the Lord, whether it is oxe, whether scheep, tho ben the Lordis part.
“‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
27 That if the beeste is vncleene, he that offride schal ayenbie by his valu, and he schal adde the fyuethe part of prijs; if he nyle ayenbie, it schal be seeld to another man, as myche euer as it is `set at valu.
Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
28 Al thing which is halewid to the Lord, whether it is man, whether beeste, whether feeld, it schal not be seeld, nether it schal mow be ayenbouyt; whateuer thing is halewid onys, it schal be hooli of the noumbre of hooli thingis to the Lord,
“‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
29 and ech halewyng which is offrid of man, schal not be ayenbouyt, but it schal die bi deeth.
“‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
30 Alle the tithis of erthe, whether of fruytis, whether of applis of trees, ben the Lordis part, and ben halewid to hym;
“‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
31 sotheli if ony man wole ayenbie hise tithis, he schal adde the fyuethe part of tho; of alle tithis,
Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
32 of scheep, and of oxen, and of geet, that passen vndur the `yerde of scheepherde, whateuer thing cometh to the tenthe part, it schal be halewid to the Lord;
Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
33 it schal not be chosun, nether good, nether yuel; nethir it schal be chaungid for another; if ony man chaungith, bothe that, that is chaungid, and that, for which it is chaungid, schal be halewid to the Lord, and it schal not be ayenbouyt.
Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
34 These ben the comaundementis whiche the Lord comaundide to Moises, and to the sones of Israel, in the hil of Synay.
Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

< Leviticus 27 >