< Leviticus 24 >

1 And the Lord spak to Moises, and seide, Comaunde thou to the sones of Israel,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 that thei brynge to thee oile of olyues, pureste oile, and briyt, to the lanternes to be ordeyned contynueli with out the veil of witnessyng,
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
3 in the tabernacle of boond of pees; and Aaron schal araye tho lanternes fro euentid `til to euentid bifor the Lord, bi religioun and custom euerlastynge in youre generaciouns;
Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
4 tho schulen be set euere on a clenneste candilstike in the siyt of the Lord.
Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
5 Also thou schalt take wheete flour, and thou schalt bake therof twelue looues, which schulen haue ech bi hem silf twei tenthe partis,
“Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
6 of whiche thou schalt sette sexe on euer eithir side, on a clenneste boord bifor the Lord;
Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
7 and thou schalt sette clereste encense on tho looues, that the looues be in to mynde of offryng of the Lord;
Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
8 bi ech sabat tho schulen be chaungid bifor the Lord, and schulen be takun of the sones of Israel bi euerlastynge boond of pees;
Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
9 and tho schulen be Aarons and hise sones, that thei ete tho in the hooli place, for it is hooli of the noumbre of hooli thingis, of the sacrifices of the Lord, bi euerlastynge lawe.
Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
10 Lo! forsothe the sone of a womman of Israel, whom sche childide of a man Egipcian, yede out among the sones of Israel, and chidde in the castels with a man of Israel,
Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
11 and whanne he hadde blasfemyd the name of the Lord, and hadde cursid the Lord, he was brouyt to Moises; forsothe his modir was clepid Salumyth, the douytir of Dabry, of the lynage of Dan;
Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
12 and thei senten hym to prisoun, til thei wisten what the Lord comaundide.
Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
13 And the Lord spak to Moises and seide,
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
14 Lede out the blasfemere without the castels, and alle men that herden, sette her hondis on his heed, and al the puple stone hym.
“Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
15 And thou schalt speke to the sones of Israel, A man that cursith his God,
Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
16 schal bere his synne, and he that blasfemeth the name of the Lord, die bi deeth; al the multitude of the puple schal oppresse hym with stoonus, whether he that blasfemede the name of the Lord is a citeseyn, whether a pilgrym, die he bi deeth.
Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
17 He that smytith and sleeth a man, die bi deeth;
“‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
18 he that smytith a beeste, yelde oon in his stide, that is, lijf for lijf.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
19 If a man yyueth a wem to ony of hise citeseyns, as he dide, so be it don to him;
Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
20 he schal restore brekyng for brekyng, iye for iye, tooth for tooth; what maner wem he yaf, he schal be compellid to suffre sich a wem.
kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
21 He that smytith werk beeste, yeelde another; he that smytith a man, schal be punyschid.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
22 Euene doom be among you, whether a pilgrym ethir a citeseyn synneth, for Y am youre Lord God.
Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And Moyses spak to the sones of Israel, and thei brouyten forth out of the castels hym that blasfemede, and oppressiden with stoonus. And the sones of Israel diden, as the Lord comaundide to Moyses.
Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.

< Leviticus 24 >