< Leviticus 23 >

1 And the Lord spak to Moises and seide, Speke thou to the sones of Israel,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 and thou schalt seye to hem, These ben the feries of the Lord, whiche ye schulen clepe hooli.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 Sixe daies ye schulen do werk, the seuenthe dai schal be clepid hooli, for it is the reste of sabat; ye schulen not do ony werk ther ynne; it is the sabat of the Lord in alle youre abitaciouns.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 These ben the hooli feries of the Lord, whiche ye owen to halewe in her tymes.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 In the firste monethe, in the fourtenthe dai of the monethe, at euentid, is pask of the Lord;
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 and in the fiftenthe dai of this monethe is the solempnyte of therf looues of the Lord; seuene daies ye schulen ete therf looues;
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 the firste dai schal be moost solempne and hooli to you; ye schulen not do ony `seruyle werk ther ynne,
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 but ye schulen offre sacrifice in fier to the Lord seuene daies; sotheli the seuenthe dai schal be more solempne and hooliere, `that is, `than the formere daies goynge bitwixe, and ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
9 And the Lord spak to Moises and seide,
Yehova anawuza Mose kuti,
10 Speke thou to the sones of Israel, and thou schalt seye to hem, Whanne ye han entrid in to the lond which Y schal yyue to you, and han rope corn, ye schulen bere handfuls of eeris of corn, the firste fruytis of youre rype corn, to the preest;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 and the preest schal reise a bundel bifor the Lord, that it be acceptable for you, in the tother dai of sabat, that is, of pask; and the preest schal halewe that bundel;
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 and in the same dai, wher ynne the handful is halewid, a lomb of o yeer without wem schal be slayn in to brent sacrifice of the Lord;
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 and fletynge offryngis schulen be offrid ther with, twei tenthe partis of wheete flour spreynt to gidere with oile, in to encense of the Lord, and swettist odour, and fletynge offryngis of wyn, the fourthe part of hyn.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 Ye schulen not ete a loof, nether a cake, nether podagis of the corn, `til to the dai in which ye schulen offre therof to youre God; it is a comaundement euerlastynge in youre generaciouns, and alle dwellyng placis.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 Therfor ye schulen noumbre fro the tother dai of sabat, in which ye offriden handfullis of firste fruytis,
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 seuene fulle woukis, til to the tothir day of fillyng of the seuenthe wouk, that is, fifti dayes; and so ye schulen
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 offre newe sacrifice to the Lord of alle youre dwelling placis, twei looues of the firste fruytis, of twei tenthe partis of flour, `diyt with soure dow, whiche looues ye schulen bake in to the firste fruytis to the Lord.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 And ye schulen offre with the looues seuene lambren of o yeer with out wem, and o calf of the droue, and twey rammes, and these schulen be in brent sacrifice, with her fletynge offryngis, in to swettest odour to the Lord.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 Ye schulen make also a buk of geet for synne, and twey lambren of o yeer, sacrificis of pesible thingis.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 And whanne the preest hath reisid tho, with the looues of firste fruytys bifor the Lord, tho schulen falle in to his vss.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 And ye schulen clepe this dai most solempne, and moost hooli; ye schulen not do ther ynne ony seruyle werk; it schal be a lawful thing euerlastynge in alle youre dwellyngis, and generaciouns.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 Forsothe aftir that ye han rope the corn of youre lond, ye schulen not kitte it `til to the ground, nether ye schulen gadere the `eeris of corn abidynge, but ye schulen leeue tho to pore men and pilgrymys; Y am `youre Lord God.
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And the Lord spak to Moises, and seide,
Yehova anawuza Mose kuti,
24 Speke thou to the sones of Israel, In the seuenthe monethe, in the firste day of the monethe, schal be sabat memorial to yow, sownynge with trumpis, and it schal be clepid hooli;
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne, and ye schulen offre brent sacrifice to the Lord.
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
26 And the Lord spak to Moises, and seide, In the tenthe day of this seuenthe monethe,
Yehova anawuza Mose kuti,
27 the day of clensyngis schal be moost solempne, and it schal be clepid hooli; and ye schulen turmente youre soulis to God, and ye schulen offre brent sacrifice to the Lord;
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 ye schulen not do ony werk in the tyme of this day, for it is the day of the clensyng, that youre Lord God be merciful to you.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Ech `man which is not tourmentid in this day, schal perische fro his puplis,
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 and Y schal do a way fro his puple that man that doith eny thing of werk in that dai;
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 therfor ye schulen not do ony thing of werk in that dai; it schal be a lawful thing euerlastynge to you in alle youre generaciouns and abitaciouns;
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 it is the sabat of restyng. Ye schulen turmente youre soulis fro the nynthe day of the monethe; fro euentid `til to euentid ye schulen halewe youre sabatis.
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
33 And the Lord spak to Moises,
Yehova anawuza Mose kuti,
34 and seide, Speke thou to the sones of Israel, Fro the fiftenthe day of this seuenthe monethe schulen be the feries of tabernaclis, in seuene daies to the Lord;
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 the firste dai schal be clepid moost solempne and moost hooli, ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne;
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 and in seuene daies ye schulen offre brent sacrifices to the Lord, and the eiythe dai schal be moost solempne and moost hooli; and ye schulen offre brent sacrifice to the Lord, for it is the day of cumpany, and of gaderyng; ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 These ben the feries of the Lord, whiche ye schulen clepe moost solempne and moost hooli; and in tho ye schulen offre offryngis to the Lord, brent sacrifices, and fletynge offeryngis, bi the custom of ech day,
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 outakun the sabatis of the Lord, and youre yiftys, and whiche ye offren bi avow, ether whiche ye yyuen bi fre wille to the Lord.
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 Therfor fro the fiftenthe day of the seuenthe monethe, whanne ye han gaderid alle the fruytis of youre lond, ye schulen halewe the feries of the Lord seuene daies; in the firste day and the eiyte schal be sabat, that is, reste.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 And ye schulen take to you in the firste day fruytis of the faireste tree, and braunchis of palm trees, and braunchis of a `tree of thicke boowis, and salewis of the rennynge streem, and ye schulen be glad bifor youre Lord God;
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 and ye schulen halewe his solempnyte seuene daies bi the yeer; it schal be a lawful thing euerlastynge in youre generaciouns. In the seuenthe monethe ye schulen halewe feestis,
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 and ye schulen dwelle in schadewynge placis seuene daies; ech man that is of the kyn of Israel, schal dwelle in tabernaclis, that youre aftercomers lerne,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 that Y made the sones of Israel to dwelle in tabernaculis, whanne Y ledde hem out of the lond of Egipt; Y am youre Lord God.
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 And Moises spak of the solempnytees of the Lord to the sones of Israel.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

< Leviticus 23 >