< Leviticus 2 >

1 Whanne a soule offrith an offryng of sacrifice to the Lord, flour of wheete schal be his offring. And he schal schede oile ther onne,
“‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
2 and he schal putte encense, and he schal bere to the sones of Aaron, preest, of whiche sones oon schal take an handful of `flour of whete, and of oile, and alle the encense; and he schal putte a memorial on the auter, in to swettest odour to the Lord.
ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
3 Forsothe that that `is residue of the sacrifice schal be Aarons and hise sones, the hooli of hooli thingis of offryngis to the Lord.
Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
4 Forsothe whanne thou offrist a sacrifice bakun in an ouene of whete flour, that is, loouys without sour dow, spreynd with oile, and therf breed sodun in watir, bawmed with oile;
“‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
5 if thin offryng is `of a friyng panne, of wheete flour spreynd with oile and without sour dow,
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
6 thou schalt departe it in smale partis, and thou schalt schede oile ther onne.
Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
7 Ellis if the sacrifice is of a gridele, euenli the whete flour schal be spreynd with oile;
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
8 which whete flour thou schalt offre to the Lord, and schalt bitake in the hondis of the preest.
Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
9 And whanne he hath offrid it, he schal take a memorial of the sacrifice, and he schal brenne it on the auter, in to `odour of swetnesse to the Lord.
Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
10 Sotheli what euer thing `is residue, it schal be Aarons and hise sones, the hooly of hooli thingis of the offryngis to the Lord.
Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
11 Ech offryng which is offrid to the Lord, schal be without sour dow, nether ony thing of sour dow, and of hony, schal be brent in the sacrifice of the Lord.
“‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
12 Ye schulen offre oneli the firste fruytis of tho, and yiftis; sotheli tho schulen not be put on the auter, in to odour of swetnesse.
Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
13 Whateuer thing of sacrifice thou schalt offre, thou schalt make it sauery with salt, nether thou schalt take awey the salt of the boond of pees of thi God fro thi sacrifice; in ech offryng thou schalt offre salt.
Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
14 Forsothe if thou offrist a yifte of the firste thingis of thi fruytis to the Lord, of `eeris of corn yit grene, thou schalt seenge tho in fier, and thou schalt breke in the maner of seedis; and so thou schalt offre thi firste fruytis to the Lord,
“‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
15 and thou schalt schede oyle theronne, and schalt putte encense, for it is the offryng of the Lord.
Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
16 Of which the preest schal brenne, in to mynde of the yifte, a part of the `seedis brokun, and of oyle, and al the encense.
Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

< Leviticus 2 >