< Leviticus 11 >

1 And the Lord spak to Moises and Aaron, and seide,
Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
2 Seie ye to the sones of Israel, Kepe ye alle thingis whiche Y wroot to you, that Y be youre God. These ben the beestis, whiche ye schulen ete, of alle lyuynge beestis of erthe;
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
3 ye schulen ete `al thing among beestis that hath a clee departid, and chewith code;
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
4 sotheli what euer thing chewith code, and hath a clee, but departith not it, as a camel and othere beestis doon, ye schulen not ete it, and ye schulen arette among vnclene thingis.
“‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
5 A cirogrille, which chewith code, and departith not the clee, is vnclene; and an hare,
Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
6 for also he chewith code, but departith not the clee;
Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
7 and a swiyn, that chewith not code, thouy he departith the clee.
Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
8 Ye schulen not ete the fleischis of these, nether ye schulen touche the deed bodies, for tho ben vnclene to you.
Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
9 Also these thingis ben that ben gendrid in watris, and is leueful to ete;
“‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 ye schulen ete al thing that hath fynnes and scalis, as wel in the see, as in floodis and stondynge watris; sotheli what euer thing of tho that ben moued and lyuen in watris, hath not fynnes and scalis, schal be abhominable, and wlatsum to you;
Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
11 ye schulen not ete the fleischis of tho, and ye schulen eschewe the bodies deed bi hem silf.
Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
12 Alle thingis in watris that han not fynnes and scalis, schulen be pollutid,
Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
13 These thingis ben of foulis whiche ye schulen not ete, and schulen be eschewid of you; an egle, and a grippe, aliete, and a kyte, and a vultur by his kynde;
“‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
14 and al of `rauyns kynde bi his licnesse;
nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
15 a strucioun,
akhungubwi a mitundu yonse,
16 and nyyt crowe, a lare, and an hauke bi his kinde;
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
17 an owle, and dippere, and ibis;
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
18 a swan and cormoraunt, and a pellican;
tsekwe, vuwo, dembo,
19 a fawcun, a iay bi his kynde; a leepwynke, and a reremows.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
20 Al thing of foulis that goith on foure feet, schal be abhomynable to you;
“‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
21 sotheli what euer thing goith on foure feet, but hath lengere hipis bihynde, bi whiche it skippith on the erthe, ye schulen ete;
Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
22 as is a bruke in his kynde, and acatus, and opymacus, and a locuste, alle bi her kynde.
Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
23 Forsothe what euer thing of briddis hath foure feet oneli, it schal be abhomynable to you;
Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
24 and who euer touchith her bodies deed bi hem silf, schal be defoulid, and `schal be vnclene `til to euentid;
“‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
25 and if it is nede, that he bere ony deed thing of these, he schal waische his clothis, and he schal be vnclene til to the goyng doun of the sunne.
Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
26 Sotheli ech beeste that hath a clee, but departith not it, nether chewith code, schal be vnclene; and what euer thing touchith it, schal be defoulid.
“‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
27 That that goith on hondis, of alle beestis that gon on foure feet, schal be vnclene; he, that touchith her bodies deed bi hem silf, schal be defoulid `til to euentid;
Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
28 and he, that berith siche deed bodies, schal waische hise clothis, and he schal be vnclene `til to euentid; for alle these thingis ben vnclene to you.
Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
29 Also these thingis schulen be arettid among defoulid thingis, of these that ben moued on erthe; a wesele, and mows, and a cocodrille, `alle bi her kynde;
“‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
30 mygal, camelion, and stellio, and lacerta, and a maldewerp.
gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
31 Alle these ben vnclene; he that touchith her bodies deed bi hem silf, schal be vnclene `til to euentid;
Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
32 and that thing schal be defoulid, on which ony thing of her bodies deed bi hem silf fallith, as wel a vessel of tree, and a cloth, as skynnes `and heiris; and in what euer thing werk is maad, it schal be dippid in watir, and tho thingis schulen be defoulid `til to euentid, and so aftirward tho schulen be clensid.
Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
33 Sotheli a vessel of erthe, in which ony thing of these fallith with ynne, schal be defoulid, and therfor it schal be brokun.
Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
34 Ech mete, which ye schulen ete, schal be vnclene, if water is sched thereon; and ech fletynge thing, which is drunkun of ech vessel, `where ynne vnclene thingis bifelden, schal be vnclene;
Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
35 and what euer thing of siche deed bodies bi hem silf felde theronne, it schal be vnclene, whether furneisis, ethir vessels of thre feet, tho schulen be destried, and schulen be vnclene.
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
36 Sotheli wellis and cisternes, and al the congregacioun of watris, schal be clene. He that touchith her bodi deed bi it silf, schal be defoulid.
Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
37 If it fallith on seed, it schal not defoule the seed;
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
38 sotheli if ony man schedith seed with watir, and aftirward the watir is touchid with deed bodies bi hem silf, it schal be defoulid anoon.
Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
39 If a beeste is deed, which it is leueful to you to ete, he that touchith the deed bodi therof schal be vnclene `til to euentid; and he that etith therof ony thing,
“‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
40 ethir berith, schal waische his clothis, and schal be vnclene `til to euentid.
Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
41 Al thing that crepith on erthe, schal be abhomynable, nether schal be takun in to mete.
“‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
42 `What euer thing goith on the brest and foure feet, and hath many feet, ethir drawun bi the erthe, ye schulen not ete, for it is abhomynable.
Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
43 Nyle ye defoule youre soulis, nether touche ye ony thing of tho, lest ye ben vnclene;
Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
44 for Y am youre Lord God; be ye hooli, for Y am hooli. Defoule ye not youre soulis in ech crepynge `beeste which is moued on erthe; for Y am the Lord,
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
45 that ladde you out of the lond of Egipt, that Y schulde be to you in to God; ye schulen be hooli, for Y am hooli.
Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
46 This is the lawe of lyuynge beestes, and of foulis, and of ech lyuynge soule which is moued in watir, and crepith in erthe;
“‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
47 that ye knowe differences of clene thing and vnclene, and that ye wite what ye schulen ete, and what ye owen forsake.
Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”

< Leviticus 11 >