< Judges 10 >

1 Aftir Abymelech roos a duyk in Israel, Thola, the sone of Phua, brother of `the fadir of Abymelech; Thola was a man of Ysachar, that dwelliden in Sanyr, of the hil of Effraym;
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
2 and he demyde Israel thre and twenti yeer, and he `was deed, and biriede in Sanyr.
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
3 His successour was Jair, a man of Galaad, that demyde Israel bi two and twenti yeer;
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
4 and he hadde thretti sones, sittynge aboue thretti coltis of femal assis, and thretti princes of citees, whiche ben clepid bi `his name, Anoth Jair, that is, the citees of Jair, `til in to present day, in the lond of Galaad.
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
5 And Jair `was deed, and biriede in a place `to which the name is Camon.
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
6 Forsothe the sones of Israel ioyneden newe synnes to elde synnes, and diden yuels in the `siyt of the Lord, and serueden to the idols of Baalym, and of Astoroth, and to the goddis of Sirie, and of Sidon, and of Moab, and of the sones of Amon, and of Filistiym; and thei leften the Lord, and worschipiden not hym.
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
7 And the Lord was wrooth ayens hem, and he bitook hem in to the hondis of Filistiym, and of the sones of Amon.
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8 And alle that dwelliden ouer Jordan in the lond of Ammorrey, which is in Galaad, weren turmentid and oppressid greetli bi eiytene yeer,
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9 in so myche that the sones of Amon, whanne thei hadden passid Jordan, wastiden Juda and Benjamyn and Effraym; and Israel was turmentid greetli.
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
10 And thei crieden to the Lord, and seiden, We han synned to thee, for we forsoken oure God, and seruyden Baalym.
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
11 To whiche the Lord spak, Whether not Egipcians, and Ammorreis, and the sones of Amon, and of Filistiym, and Sidonyes,
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
12 and Amalech, and Canaan, oppressiden you, and ye crieden to me, and Y delyuerede you fro `the hondis of hem?
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
13 And netheles ye forsoken me, and worschipiden alien goddis; therfor Y schal not adde, that Y delyuere you more.
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
14 Go ye, and clepe goddis whiche ye han chose; delyuere thei you in the tyme of angwisch.
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
15 And the sones of Israel seiden to the Lord, We han synned; yelde thou to vs what euer thing plesith thee; oneli delyuere vs now.
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
16 And thei seiden these thingis, and castiden forth fro her coostis alle the idols of alien goddis, and serueden the Lord; which hadde `rewthe, ether compassioun, on the `wretchidnessis of hem.
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
17 And so the sones of Amon crieden togidere, that is, clepyden hem silf togidere to batel, and excitiden ayens Israel, and settiden tentis in Galaad, `ayens whiche the sones of Israel weren gaderid, and settiden tentis in Masphat.
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
18 And the princes of Galaad seiden ech to hise neiyboris, He, that bigynneth first of vs to fiyte ayens the sones of Amon, schal be duyk of the puple of Galaad.
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

< Judges 10 >