< Joshua 5 >

1 Therfor aftir that alle kyngis of Ammorreys herden, that dwelliden ouer Jordan at the west coost, and alle the kyngis of Canaan, that weldiden nyy places of the greet see, that the Lord hadden dried the flowyngis of Jordan bifor the sones of Israel, til thei passiden, the herte of hem was failid, and spirit dwellide not in hem, dredynge the entring of the sones of Israel.
Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
2 In that tyme the Lord seide to Josue, Make to thee knyues of stoon, and circumside thou the sones of Israel, in the secunde tyme.
Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
3 Josue dide tho thingis whiche the Lord comaundide, and he circumside the sones of Israel in the `hil of prepucies.
Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
4 Sotheli this is the cause of the secunde circumcisioun; al the puple of male kynde, that yede out of Egipt, alle men fiyteris, weren deed in deseert bi the lengeste cumpassis of weie,
Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
5 whiche alle weren circumsidid. Sotheli the puple
Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
6 that was borun in deseert bi fourti yeer, in the weie of broddeste wildirnesse, was vncircumsidid til thei weren waastid, that herden not the `vois of the Lord, and to whiche he swoor bifore, that he schulde schewe to hem the lond flowynge with mylk and hony.
Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
7 The sones of hem camen aftirward in to the place of fadris, and thei weren circumsidid of Josue; whiche, as thei weren borun, weren in prepucie, nether ony man hadde circumsidid hem in the weie.
Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
8 Forsothe aftir that alle weren circumsidid, thei dwelliden in the same place of tentis, til thei weren heelid.
Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
9 And the Lord seide to Josue, To dai Y haue take awei fro you the schenschip of Egipt. And the name of that place was clepid Galgala, `til in to present dai.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
10 And the sones of Israel dwelliden in Galgalis, and maden pask in the fourtenthe dai of the monethe at euentide, in the feeldi places of Jerico;
Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
11 and `thei eten of the fruytis of the lond `in the tothir day, therf looues, and potage of the same yeer, `ether cornys seengid and frotid in the hond.
Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
12 And manna failide aftir that thei eten of the fruytis of the lond; and the sones of Israel vsiden no more that mete, but thei eten of the fruytis of present yeer of the lond of Canaan.
Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
13 Sothely whanne Josue was in the feeld of the cite of Jerico, he reiside the iyen, and siy a man stondynge ayens hym, and holdynge a drawun swerd; and Josue yede out to hym, and seide, Art thou oure, ethir `of aduersaries?
Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
14 To whom he answeride, Nay, but Y am prince of the `hoost of the Lord, and now Y come. Josue felde lowe to erthe, and worschipide, and seide, What spekith my Lord to his seruaunt?
Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
15 He seide, Vnlace thi schoo fro thi feet, for the place, in which thou stondist, is hooli. And Josue dide, as it was comaundid to hym.
Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.

< Joshua 5 >