< Joshua 14 >

1 This `thing it is, which the sones of Israel weldiden in the lond of Canaan, which lond Eleazar the preest, and Josue, the sone of Nun, and the princes of meynees bi the lynagis of Israel yauen to hem,
Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
2 and departiden alle thingis bi lot, as the Lord comaundide in the hond of Moises, to nyne lynagis and the half lynage.
Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
3 For Moises hadde youe to `the twey lynagis and to the half lynage `possessioun ouer Jordan; without the Leuytis, that token no thing of the lond among her britheren;
Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
4 but the sones of Joseph weren departid in to twei lynagis, of Manasses and of Effraym, and `weren eiris in to the place of hem. And `the Leuytis token noon other part in the lond, no but citees to dwelle, and the subarbis of tho to werke beestis and her scheep to be fed.
Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
5 As the Lord comaundide to Moises, so the sones of Israel diden, and departiden the lond.
Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 And so the sones of Juda neiyiden to Josue in Galgalis; and Caleph, the sone of Jephone, of Ceneth, spak to him, Thou knowist, what the Lord spak to Moises, the man of God, of me and of thee in Cades Barne.
Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
7 Y was of fourti yeer, whanne Moises, `seruaunt of the Lord, sente me fro Cades Barne, that Y schulde biholde the lond, and Y teelde to hym that, that semyde soth to me.
Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
8 Forsothe my britheren, thats tieden with me, discoumfortiden the herte of the puple, and neuertheles Y suede my Lord God.
Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
9 And Moises swoor in that dai, and seide, The lond, which thi foot trad, schal be thi possessioun, and of thi sones withouten ende; for thou suedist thi Lord God.
Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
10 Sotheli the Lord grauntide lijf to me, as he bihiyte, `til in to present dai. Fourti yeer and fyue ben, sithen the Lord spak this word to Moises, whanne Israel yede bi the wildirnesse. To dai Y am of `foure scoor yeer and fyue,
“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
11 and Y am as myyti, as Y was myyti in that time, whanne Y was sent to aspie; the strengthe `of that tyme dwellith stabli in me `til to dai, as wel to fiyte, as to go.
Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
12 Therfor yyue thou to me this hil, which the Lord bihiyte to me, while also thou herdist, in which hil ben Enachym, and grete `citees, and strengthid; if in hap the Lord is with me, and Y mai do hem awei, as he bihiyte to me.
Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
13 And Josue blesside hym, and yaf to hym Ebron in to possessioun.
Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
14 And fro that tyme Ebron was to Caleph, sone of Jephone, of Cenez, `til in to present dai; for he suede the Lord God of Israel.
Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
15 The name of Ebron was clepid bifore Cariatharbe. Adam, the gretteste, was set there in the lond of Enachym; and the lond ceesside fro batels.
(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.

< Joshua 14 >