< Job 33 >

1 Therfor, Joob, here thou my spechis, and herkene alle my wordis.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Lo! Y haue openyd my mouth, my tunge schal speke in my chekis.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Of symple herte ben my wordis, and my lippis schulen speke clene sentence.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 The spirit of God made me, and the brething of Almyyti God quykenyde me.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 If thou maist, answere thou to me, and stoonde thou ayens my face.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Lo! God made me as and thee; and also Y am formyd of the same cley.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Netheles my myracle make thee not afeerd, and myn eloquence be not greuouse to thee.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Therfor thou seidist in myn eeris, and Y herde the vois of thi wordis;
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Y am cleene, and with out gilt, and vnwemmed, and wickidnesse is not in me.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 `For God foond querels in me, therfor he demyde me enemy to hym silf.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 He hath set my feet in a stok; he kepte alle my pathis.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Therfor this thing it is, in which thou art not maad iust; Y schal answere to thee, that God is more than man.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Thou stryuest ayenus God, that not at alle wordis he answeride to thee.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 God spekith onys, and the secounde tyme he rehersith not the same thing.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 God spekith bi a dreem in the visioun of nyyt, whanne sleep fallith on men, and thei slepen in the bed.
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Thanne he openith the eeris of men, and he techith hem, `and techith prudence;
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 that he turne awei a man fro these thingis whiche he made, and delyuere hym fro pride; delyuerynge his soule fro corrupcioun,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 and his lijf, that it go not in to swerd.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Also God blameth a synnere bi sorewe in the bed, and makith alle the boonys of hym `to fade.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Breed is maad abhomynable to hym in his lijf, and mete desirable `bifor to his soule.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 His fleisch schal faile for rot, and hise boonys, that weren hilid, schulen be maad nakid.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 His soule schal neiye to corrupcioun, and his lijf to thingis `bryngynge deeth.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 If an aungel, oon of a thousynde, is spekynge for hym, that he telle the equyte of man, God schal haue mercy on hym,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 and schal seie, Delyuere thou hym, that he go not doun in to corrupcioun; Y haue founde in what thing Y schal do merci to hym.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 His fleisch is wastid of turmentis; turne he ayen to the daies of his yonge wexynge age.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 He schal biseche God, and he schal be quemeful to hym; and he schal se his face in hertly ioye, and he schal yelde to man his riytfulnesse.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 He schal biholde men, and he schal seie, Y haue synned, and verili Y haue trespassid; and Y haue not resseyued, as Y was worthi.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 For he delyueride his soule, that it schulde not go in to perischyng, but that he lyuynge schulde se liyt.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Lo! God worchith alle these thingis in thre tymes bi alle men;
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 that he ayen clepe her soulis fro corrupcioun, and liytne in the liyt of lyuynge men.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Thou, Joob, perseyue, and here me, and be thou stille, the while Y speke.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Sotheli if thou hast what thou schalt speke, answere thou to me, speke thou; for Y wole, that thou appere iust.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 That if thou hast not, here thou me; be thou stille, and Y schal teche thee wisdom.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >