< Job 31 >

1 I made couenaunt with myn iyen, that Y schulde not thenke of a virgyn.
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 For what part schulde God aboue haue in me, and eritage Almyyti God of hiye thingis?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Whether perdicioun is not to a wickid man, and alienacioun of God is to men worchynge wickidnesse?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Whether he biholdith not my weies, and noumbrith alle my goyngis?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 If Y yede in vanyte, and my foot hastide in gile,
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 God weie me in a iust balaunce, and knowe my symplenesse.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 If my step bowide fro the weie; if myn iye suede myn herte, and a spotte cleuede to myn hondis;
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 sowe Y, and another ete, and my generacioun be drawun out bi the root.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 If myn herte was disseyued on a womman, and if Y settide aspies at the dore of my frend; my wijf be the hoore of anothir man,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 and othir men be bowid doun on hir.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 For this is vnleueful, and the moost wickidnesse.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Fier is deourynge `til to wastyng, and drawynge vp bi the roote alle generaciouns.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 If Y dispiside to take doom with my seruaunt and myn hand mayde, whanne thei stryueden ayens me.
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 What sotheli schal Y do, whanne God schal rise to deme? and whanne he schal axe, what schal Y answere to hym?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Whether he, that wrouyte also hym, made not me in the wombe, and o God formede me in the wombe?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 If Y denyede to pore men that, that thei wolden, and if Y made the iyen of a wydewe to abide;
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 if Y aloone eet my mussel, and a faderles child eet not therof;
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 for merciful doyng encreesside with me fro my yong childhed, and yede out of my modris wombe with me;
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 if Y dispiside a man passynge forth, for he hadde not a cloth, and a pore man with out hilyng;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 if hise sidis blessiden not me, and was not maad hoot of the fleeces of my scheep;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 if Y reiside myn hond on a fadirles child, yhe, whanne Y siy me the hiyere in the yate;
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 my schuldre falle fro his ioynt, and myn arm with hise boonys be al to-brokun.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 For euere Y dredde God, as wawis wexynge gret on me; and `Y myyte not bere his birthun.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 If Y gesside gold my strengthe, and if Y seide to purid gold, Thou art my trist;
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 if Y was glad on my many ritchessis, and for myn hond foond ful many thingis;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 if Y siy the sunne, whanne it schynede, and the moone goynge clereli;
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 and if myn herte was glad in priuyte, and if Y kisside myn hond with my mouth;
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 which is the moost wickidnesse, and deniyng ayens hiyeste God;
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 if Y hadde ioye at the fallyng of hym, that hatide me, and if Y ioide fulli, that yuel hadde founde hym;
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 for Y yaf not my throte to do synne, that Y schulde asaile and curse his soule;
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 if the men of my tabernacle seiden not, Who yyueth, that we be fillid of hise fleischis? a pilgryme dwellide not with outforth;
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 my dore was opyn to a weiegoere;
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 if Y as man hidde my synne, and helide my wickidnesse in my bosum;
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 if Y dredde at ful greet multitude, and if dispisyng of neyyboris made me aferd; and not more Y was stille, and yede not out of the dore;
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 who yyueth an helpere to me, that Almyyti God here my desire? that he that demeth,
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 write a book, that Y bere it in my schuldre, and cumpasse it as a coroun to me?
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Bi alle my degrees Y schal pronounce it, and Y schal as offre it to the prynce.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 If my lond crieth ayens me, and hise forewis wepen with it;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 if Y eet fruytis therof with out money, and Y turmentide the soule of erthetileris of it;
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 a brere growe to me for wheete, and a thorn for barli.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >