< Job 29 >

1 Also Joob addide, takynge his parable, and seide,
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Who yyueth to me, that I be bisidis the elde monethis, bi the daies in whiche God kepte me?
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 Whanne his lanterne schynede on myn heed, and Y yede in derknessis at his liyt.
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 As Y was in the daies of my yongthe, whanne in priuete God was in my tabernacle.
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 Whanne Almyyti God was with me, and my children weren in my cumpas;
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 whanne Y waischide my feet in botere, and the stoon schedde out to me the stremes of oile;
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 whanne Y yede forth to the yate of the citee, and in the street thei maden redi a chaier to me.
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 Yonge men, `that is, wantoun, sien me, and weren hid, and elde men risynge vp stoden;
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 princes ceessiden to speke, and puttiden the fyngur on her mouth;
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 duykis refreyneden her vois, and her tunge cleuyde to her throte.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 An eere herynge blesside me, and an iye seynge yeldide witnessyng to me;
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 for Y hadde delyueride a pore man criynge, and a fadirles child, that hadde noon helpere.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 The blessyng of a man `to perische cam on me, and Y coumfortide the herte of a widewe.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Y was clothid with riytfulnesse; and Y clothide me as with a cloth, and with my `doom a diademe.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Y was iye `to a blynde man, and foot to a crokyd man.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Y was a fadir of pore men; and Y enqueride most diligentli the cause, which Y knew not.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Y al tobrak the grete teeth of the wickid man, and Y took awei prey fro hise teeth.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 And Y seide, Y schal die in my nest; and as a palm tre Y schal multiplie daies.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 My roote is openyde bisidis watris, and deew schal dwelle in my repyng.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 My glorie schal euere be renulid, and my bouwe schal be astorid in myn hond.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Thei, that herden me, abiden my sentence; and thei weren ententif, and weren stille to my counsel.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Thei dursten no thing adde to my wordis; and my speche droppide on hem.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 Thei abididen me as reyn; and thei openyden her mouth as to the softe reyn `comynge late.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 If ony tyme Y leiyide to hem, thei bileueden not; and the liyt of my cheer felde not doun in to erthe.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 If Y wolde go to hem, Y sat the firste; and whanne Y sat as kyng, while the oost stood aboute, netheles Y was comfortour of hem that morenyden.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >