< Job 2 >

1 Forsothe it was doon, whanne in sum dai the sones of God `weren comun, and stoden bifor the Lord, and Sathan `was comun among hem, and stood in his siyt,
Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
2 that the Lord seide to Sathan, Fro whennus comest thou? Which answeride, and seide, Y haue cumpassid the erthe, `and Y haue go thury it.
Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
3 And the Lord seide to Sathan, Whethir thou hast biholde my seruaunt Joob, that noon in erthe is lijk hym; he is a symple man, and riytful, and dredynge God, and goynge awei fro yuel, and yit holdynge innocence? `But thou hast moued me ayens him, that `Y schulde turmente hym in veyn.
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
4 To whom Sathan answeride, and seide, `A man schal yyue skyn for skyn, and alle thingis that he hath for his lijf;
Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
5 `ellis sende thin hond, and touche his boon and fleisch, and thanne thou schalt se, that he schal curse thee in the face.
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
6 Therfor the Lord seide to Sathan, Lo! he is in `thin hond; netheles kepe thou his lijf.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
7 Therfor Sathan yede out fro the face of the Lord, and smoot Joob with `a ful wickid botche fro the sole of the foot `til to his top;
Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
8 which Joob schauyde the quytere with a schelle, `and sat in the dunghil.
Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
9 Forsothe his wijf seide to hym, Dwellist thou yit in thi symplenesse? Curse thou God, and die.
Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
10 And Joob seide, Thou hast spoke as oon of the fonned wymmen; if we han take goodis of the hond of the Lord, whi forsothe suffren we not yuels? In alle these thingis Joob synnede not in hise lippis.
Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
11 Therfor thre frendis of Joob herden al the yuel, that hadde bifelde to hym, and camen ech man fro his place, Eliphath Temanytes, and Baldach Suythes, and Sophar Naamathites; for thei `hadden seide togidere to hem silf, that thei wolden come togidere, and visite hym, and coumforte.
Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
12 And whanne thei hadden reisid afer `her iyen, thei knewen not hym; and thei crieden, and wepten, and to-renten her clothis, and spreynten dust on her heed `in to heuene.
Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
13 And thei saten with hym in the erthe seuene daies and seuene nyytis, and no man spak a word to hym; for thei sien, that his sorewe was greet.
Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.

< Job 2 >