< Job 13 >

1 Lo! myn iye siy alle thingis, and myn eere herde; and Y vndurstood alle thingis.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Euene with youre kunnyng also Y kan, and Y am not lowere than ye.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 But netheles Y schal speke to Almyyti God, and Y coueite to dispute with God;
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 and firste Y schewe you makeris of leesyng, and louyeris of weyward techyngis.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 And `Y wolde that ye weren stille, that ye weren gessid to be wise men.
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Therfor here ye my chastisyngis; and perseyue ye the doom of my lippis.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Whether God hath nede to youre leesyng, that ye speke gilis for hym?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Whether ye taken his face, and enforsen to deme for God?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Ethir it schal plese hym, fro whom no thing mai be hid? Whether he as a man schal be disseyued with youre falsnessis?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 He schal repreue you; for ye taken his face in hiddlis.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Anoon as he schal stire hym, he schal disturble you; and his drede schal falle on you.
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Youre mynde schal be comparisound to aische; and youre nollis schulen be dryuun in to clei.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Be ye stille a litil, that Y speke, what euer thing the mynde hath schewid to me.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Whi to-rende Y my fleischis with my teeth, and bere my lijf in myn hondis?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Yhe, thouy God sleeth me, Y schal hope in hym; netheles Y schal preue my weies in his siyt.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 And he schal be my sauyour; for whi ech ypocrite schal not come in his siyt.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Here ye my word, and perseyue ye with eeris derke and harde figuratif spechis.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Yf Y schal be demed, Y woot that Y schal be foundun iust.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Who is he that is demed with me? Come he; whi am Y stille, and am wastid?
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Do thou not to me twei thingis oneli; and thanne Y schal not be hid fro thi face.
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Make thin hond fer fro me; and thi drede make not me aferd.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Clepe thou me, and Y schal answere thee; ethir certis Y schal speke, and thou schalt answere me.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Hou grete synnes and wickidnessis haue Y? Schewe thou to me my felonyes, and trespassis.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Whi hidist thou thi face, and demest me thin enemy?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Thou schewist thi myyt ayens a leef, which is rauyschid with the wynd; and thou pursuest drye stobil.
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 For thou writist bitternessis ayens me; and wolt waste me with the synnes of my yong wexynge age.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Thou hast set my foot in a stok, and thou hast kept alle my pathis; and thou hast biholde the steppis of my feet.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 And Y schal be wastid as rot, and as a cloth, which is etun of a mouyte.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Job 13 >