< Jeremiah 9 >

1 Who schal yyue watir to myn heed, and a welle of teeris to myn iyen? And Y schal biwepe dai and niyt the slayn men of the douyter of my puple.
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Who schal yyue me in to a wildirnesse of dyuerse weigoeris? And I schal forsake my puple, and Y schal go awei fro hem. For whi alle ben auowteris, and the cumpenyes of trespassouris ayens the lawe;
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 and thei helden forth her tunge as a bouwe of leesyng, and not of treuthe Thei ben coumfortid in erthe, for thei yeden out fro yuel to yuel, and thei knewen not me, seith the Lord.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Ech man kepe hym fro his neiybore, and haue no trist in ony brother of hym; for whi ech brother disseyuyng schal disseyue, and ech frend schal go gilefuli.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 And a man schal scorne his brother, and schal not speke treuthe; for thei tauyten her tunge to speke leesyng; thei traueliden to do wickidli.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Thi dwellyng is in the myddis of gile; in gile thei forsoken to knowe me, seith the Lord.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Therfor the Lord of oostis seith these thingis, Lo! Y schal welle togidere, and Y schal preue hem; for whi what other thing schal Y do fro the face of the douyter of my puple?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 The tunge of hem is an arowe woundynge, and spak gile; in his mouth he spekith pees with his frend, and priueli he settith tresouns to hym.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Whether Y schal not visite on these thingis, seith the Lord, ether schal not my soule take veniaunce on siche a folc?
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 On hillis Y schal take wepyng and mournyng, and weilyng on the faire thingis of desert, for tho ben brent; for no man is passynge forth, and thei herden not the vois of hym that weldith; fro a brid of the eir `til to scheep, tho passiden ouer, and yeden awei.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 And Y schal yyue Jerusalem in to heepis of grauel, and in to dennes of dragouns; and Y schal yyue the citees of Juda in to desolacioun, for ther is no dwellere.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Who is a wise man that schal vndurstonde these thingis, and to whom the word of the mouth of the Lord schal be maad, that he telle this? Whi the erthe perischide, it is brent as desert, for noon is that passith?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 And the Lord seide, For thei forsoken my lawe, which Y yaf to hem, and thei herden not my vois, and thei yeden not therynne;
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 and thei yeden aftir the schrewidnesse of her herte, and aftir Baalym, which thei lerneden of her fadris;
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 therfor the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Lo! Y schal fede this puple with wermod, and Y schal yyue to hem drynke the watir of galle.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 And Y schal scatere hem among hethene men, whiche thei and her fadris knewen not; and Y schal sende swerd aftir hem, til thei ben wastid.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Biholde ye, and clepe ye wymmen `that weilen, and come thei; and sende ye to tho wymmen that ben wise, and haste thei.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Haste thei, and take thei weilynge on you; youre iyen brynge doun teeris, and youre iyelidis flowe with watris;
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 for the vois of weilyng is herd fro Sion. Hou ben we distried, and schent greetli? for we han forsake the lond, for oure tabernaclis ben forsakun.
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Therfor, wymmen, here ye the word of the Lord, and youre eeris take the word of his mouth; and teche ye youre douytris weilyng, and ech womman teche hir neiybore mournyng.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 For whi deth stiede bi youre wyndows, it entride in to youre housis, to leese litle children with outforth, and yonge men fro the stretis.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Speke thou, the Lord seith, these thingis, And the deed bodi of a man schal fal doun as a toord on the face of the cuntrei, and as hei bihynde the bak of the mowere, and noon is that gaderith.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 The Lord seith these thingis, A wise man haue not glorie in his wisdom, and a strong man haue not glorie in his strengthe, and a riche man haue not glorie in hise richessis; but he that hath glorie,
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 haue glorie in this, to wite and knowe me, for Y am the Lord, that do merci and dom and riytfulnesse in erthe. For whi these thingis plesen me, seith the Lord.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Lo! daies comen, seith the Lord, and Y schal visite on ech man that hath prepucie vncircumcidid; on Egipt,
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 and on Juda, and on Edom, and on the sones of Amon, and on Moab, and on alle men that ben clippid on long heer, and dwellen in desert; for whi alle hethene men han prepucie, forsothe al the hous of Israel ben vncircumcidid in herte.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremiah 9 >