< Jeremiah 44 >

1 The word that was maad to Jeremye, and to alle the Jewis, that dwelliden in the lond of Egipt, dwellinge in Magdalo, and in Taphnys, and in Memphis, and in the lond of Phatures,
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 and seide, The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Ye sien al this yuel, which Y brouyte on Jerusalem, and on alle the citees of Juda; and lo! tho ben forsakun to dai, and no dwellere is in tho;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 for the malice which thei diden, to terre me to wrathfulnesse, and that thei yeden, and maden sacrifice, and worschipiden alien goddis, whiche thei knewen not, bothe ye, and thei, and youre fadris.
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 And Y sente to you alle my seruauntis profetis; and Y roos bi nyyte, and sente, and seide, Nyle ye do the word of sich abhomynacioun.
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 And thei herden not, nether bowiden doun her eere, that thei schulen be conuertid fro her yuels, and schulden not make sacrifice to alien goddis.
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 And myn indignacioun and my strong veniaunce is wellid togidere, and is kindlid in the citees of Juda, and in the stretis of Jerusalem; and tho ben turned in to wildirnesse, and wastnesse, bi this dai.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 And now the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Whi doon ye this greet yuel ayens youre soulis, that a man of you perische and a womman a litil child and soukynge perische, fro the myddis of Juda, nether ony residue thing be left in you,
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 that terre me to wraththe bi the werkis of youre hondis, in makynge sacrifice to alien goddis in the lond of Egipt, in to which ye entriden, that ye dwelle there, and that ye perische, and be in to cursyng, and in to schenschipe to alle the folkis of erthe?
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Whether ye han foryete the yuels of youre fadris, and the yuels of the kingis of Juda, and the yuels of her wiues, and youre yuels, and the yuels of youre wyues, whiche thei diden in the lond of Juda, and in the cuntreis of Jerusalem?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 Thei ben not clensid `til to this dai, and thei dredden not, and thei yeden not in the lawe of the Lord, and in myn heestis, whiche Y yaf bifore you, and bifore youre fadris.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 Therfor the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Lo! Y schal sette my face in you in to yuel,
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 and Y schal leese al Juda, and Y schal take the remenauntis of Juda, that settiden her faces, to go in to the lond of Egipt, and to dwelle there; and alle schulen be waastid in the lond of Egipt, thei schulen falle doun bi swerd, and schulen be wastid in hungur, fro the leeste `til to the mooste, thei schulen die bi swerd and hungur, and schulen be in to swering, and in to myracle, and in to cursyng, and in to schenschipe.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 And Y schal visite on the dwelleris of Egipt, as Y visitide on Jerusalem, in swerd, and in hungur, and in pestilence.
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 And noon schal be, that schal ascape, and be residue of the remenauntis of Jewis, that goen to be pilgrimys in the lond of Egipt, and to turne ayen to the lond of Juda, to which thei reisen her soulis, that thei turne ayen, and dwelle there; thei schulen not turne ayen thidir, no but thei that fledden.
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 Forsothe alle men answeriden to Jeremye, and wisten, that her wyues maden sacrifice to alien goddis, and alle wymmen, of whiche a greet multitude stood, and alle the puple of dwelleris in the lond of Egipt, in Fatures, and seiden,
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 We schulen not here of thee the word which thou spekist to vs in the name of oure Lord God,
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 but we doynge schulen do ech word that schal go out of oure mouth, that we make sacrifice to the queen of heuene, and that we offre to it moist sacrifices, as we diden, and oure fadris, oure kingis, and oure princes, in the citees of Juda, and in the stretis of Jerusalem; and we weren fillid with looues, and it was wel to vs, and we sien noon yuel.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 But fro that tyme, in which we ceessiden to make sacrifice to the queen of heuene, and to offre to it moist sacrifices, we hadden nede to alle thingis, and we weren wastid bi swerd and hungur.
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 That if we maken sacrifice to the queen of heuene, and offren to it moist sacrifices, whether withouten oure hosebondis we maden to it cakis, to worschipe it, and looues to be offrid?
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 And Jeremye seide to al the puple, ayens the men, and ayens the wymmen, and ayens al the puple, that answeriden to hym the word, and he seide,
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 Whether not the sacrifice which ye sacrifisiden in the citees of Juda, and in the stretis of Jerusalem, ye, and youre fadris, youre kyngis, and youre princes, and the puple of the lond, terriden God to veniaunce? The Lord hadde mynde on these thingis, and it stiede on his herte;
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 and the Lord myyte no more bere, for the malice of youre studies, and for abhomynaciouns whiche ye diden. And youre lond is maad in to desolacioun, and in to wondryng, and in to curs, for no dwellere is, as this dai is.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Therfor for ye maden sacrifice to idols, and synneden to the Lord, and herden not the vois of the Lord, and yeden not in the lawe, and in the comandementis, and in the witnessis of hym, therfor these yuels bifellen to you, as this dai is.
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 Forsothe Jeremye seide to al the puple, and to alle the wymmen, Al Juda, that ben in the lond of Egipt, here ye the word of the Lord.
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, and spekith, Ye and youre wyues spaken with youre mouth, and filliden with youre hondis, and seiden, Make we oure vowis whiche we vowiden, that we make sacrifice to the queen of heuene, and offre to it moist sacrifices; ye filliden youre vowis, and diden tho in werk.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 Therfor, al Juda, that dwellen in the lond of Egipt, here ye the word of the Lord; Lo! Y swoor in my greet name, seith the Lord, that my name schal no more be clepid bi the mouth of ech man Jew, seiynge, The Lord God lyueth, in al the lond of Egipt.
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Lo! Y schal wake on hem in to yuel, and not in to good; and alle the men of Juda, that ben in the lond of Egipt, schulen be waastid, bi swerd and hungur, til thei be wastid outerli.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 And a fewe men that fledden the swerd, schulen turne ayen fro the lond of Egipt in to the lond of Juda; and alle the remenauntis of Juda, of hem that entren in to the lond of Egipt, to dwelle there, schulen wite, whos word schal be fillid, myn ether hern.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 And this schal be a signe to you, seith the Lord, that Y schal visite on you in this place, that ye wite, that verili my wordis schulen be fillid ayens you in to yuel.
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 The Lord seith these thingis, Lo! Y schal bitake Farao, the kyng of Egipt, in to the hond of hise enemyes, and in to the hond of hem that seken his lijf, as Y bitook Sedechie, the kyng of Juda, in to the hond of Nabugodonosor, kyng of Babiloyne, his enemye, and sekynge his lijf.
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”

< Jeremiah 44 >