< Jeremiah 33 >

1 And the word of the Lord was maad to Jeremye, in the secounde tyme, whanne he was closid yit in the porche of the prisoun, and seide,
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 The Lord seith these thingis, The Lord is name of hym, that schal do, and fourme, and make redi that thing;
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Crye thou to me, and Y schal here thee, and Y schal telle to thee grete thingis, and stidfast, whiche thou knowist not.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 For the Lord God of Israel seith these thingis to the housis of this citee, and to the housis of the kyng of Juda, that ben distried, and to the strengthingis,
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 and to the swerd of men comynge to fiyte with Caldeis, and to fille tho housis with careyns of men, which Y smoot in my strong veniaunce, and in myn indignacioun; and Y hidde my face fro this citee, for al the malice of hem.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Lo! Y schal close togidere to hem a wounde and helthe, and Y schal make hem hool, and Y schal schewe to hem the bisechyng of pees and of treuthe;
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 and Y schal conuerte the conuersioun of Juda, and Y schal conuerte the conuersioun of Jerusalem, and Y schal bilde hem, as at the bigynnyng.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 And Y schal clense hem fro al her wickidnesse, in which thei synneden to me, and Y schal be merciful to alle the wickidnessis of hem, in which thei trespassiden to me, and forsoken me.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 And thei schulen be to me in to a name, and in to ioye, and in to heriyng, and in to ful out ioiyng to alle folkis of erthe, that herden alle the goodis whiche Y schal do to hem; and thei schulen drede, and schulen be disturblid in alle goodis, and in al the pees, which Y schal do to hem.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 The Lord seith these thingis, Yit in this place, which ye seien to be forsakun, for no man is nether beeste in the citees of Juda, and in the yatis of Jerusalem, that ben desolat, without man, and with out dwellere,
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 and with out beeste, the vois of ioye schal be herd, and the vois of gladnesse, the vois of spouse, and the vois of spousesse, the vois of men, seiynge, Knowleche ye to the Lord of oostis, for the Lord is good, for his merci is with outen ende, and of men berynge vowis in to the hous of the Lord; for Y schal brynge ayen the conuersioun of the lond, as at the bigynnyng, seith the Lord.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 The Lord of oostis seith these thingis, Yit in this forsakun place, with out man, and with out beeste, and in alle citees therof, schal be a dwellyng place of scheepherdis, of flockis ligynge.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 And in the citees in hilli places, and in the citees in feeldi places, and in the citees that ben at the south, and in the lond of Beniamyn, and in the cumpas of Jerusalem, and in the citees of Juda, yit flockis schulen passe, at the hond of the noumbrere, seith the Lord.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Lo! daies comen, seith the Lord, and Y schal reise the good word, which Y spak to the hous of Israel, and to the hous of Juda.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 In tho daies, and in that tyme, Y schal make the seed of riytfulnesse to buriowne to Dauid, and he schal make doom and riytfulnesse in erthe.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 In tho daies Juda schal be sauyd, and Israel schal dwelle tristili; and this is the name which thei schulen clepe hym, Oure riytful Lord.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 For the Lord seith these thingis, A man of Dauid schal not perische, that shal sitte on the trone of the hous of Israel;
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 and of preestis and dekenes a man schal not perische fro my face, that schal offre brent sacrifices, and brenne sacrifice, and sle sacrifice, in alle daies.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 And the word of the Lord was maad to Jeremye,
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 and seide, The Lord seith these thingis, If my couenaunt with the dai and my couenaunt with the niyt mai be maad voide, that the dai and the niyt be not in his tyme;
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 and my couenaunt with Dauid, my seruaunt, mai be voide, that of hym be no sone, that schal regne in his trone, and no dekenes, and preestis, my mynistris;
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 as the sterris of heuene moun not be noumbrid, and the grauel of the see mai not be metun, so Y schal multiplie the seed of Dauid, my seruaunt, and dekenes, my mynystris.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 And the word of the Lord was maad to Jeremye, and seide, Whether thou hast not seyn,
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 that this puple spak, seiynge, Twei kynredis whiche the Lord chees, ben cast awei, and thei dispisiden my puple, for it is no more a folc bifore hem.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 The Lord seith these thingis, If Y settide not my couenaunt bitwixe dai and niyt, and if Y settide not lawis to heuene and erthe;
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 sotheli and Y schal caste awei the seed of Jacob, and of Dauid, my seruaunt, that Y take not of the seed of hym princes, of the seed of Abraham, of Isaac, and of Jacob; for Y schal brynge ayen the conuersioun of hem, and Y schal haue merci on hem.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”

< Jeremiah 33 >