< Jeremiah 3 >

1 It is seid comunli, If a man forsakith his wijf, and sche go awei fro hym, and be weddid to an othere hosebonde, whether he schal turne ayen more to hir? whether thilke womman schal not be defoulid, and maad vncleene? Forsothe thou hast do fornycacioun with many loueris; netheles turne thou ayen to me, `seith the Lord, and Y schal resseyue thee.
“Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
2 Reise thin iyen in to streiyt, and se, where thou art not cast doun. Thou hast setun in weies, abidynge hem as a theef in wildirnesse, and thou hast defoulid the erthe in thi fornicaciouns and in thi malices.
“Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
3 Wherfor the dropis of reynes weren forbodun, and no late reyn was. The forhed of a womman hoore is maad to thee; thou noldist be aschamed.
Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
4 Nameli fro this tyme forth clepe thou me, Thou art my fadir, the ledere of my virginyte.
Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
5 Whether thou schalt be wrooth with outen ende, ether schalt contynue in to the ende? Lo! thou hast spoke, and hast do yuels, and thou were myyti. And for wordis of penaunce thou blasfemydist bi wordis of pride; and thou fillidist thin yuel thouyt, and schewidist thi strengthe ayens thi hosebonde, that thou maist do that thing that thou tretidist bi word.
kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
6 And the Lord seide to me, in the daies of Josie, the kyng, Whether thou hast seyn what thing the aduersarie, Israel, hath do? Sche yede to hir silf on ech hiy hil, and vndur ech tre ful of boowis, and dide fornycacioun there.
Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
7 And Y seide, whanne sche hadde do alle these thingis, Turne thou ayen to me; and sche turnede not ayen. And hir sistir, Juda, brekere of the lawe,
Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
8 siy, that for the aduersarie, Israel, dide auowtrie, Y hadde left hir, and Y hadde youe to hir a libel of forsakyng; and Juda, hir sistir, brekere of the lawe, dredde not, but also sche yede, and dide fornycacioun.
Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
9 And bi liytnesse of hir fornicacioun sche defoulide the erthe, and dide auowtrie with a stoon, and with a tree.
Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
10 And in alle these thingis hir sistir, Juda, brekere of the lawe, turnede not ayen to me, in al hir herte, but in a leesyng, seith the Lord God.
Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
11 And the Lord seide to me, The aduersarie, Israel, hath iustified hir soule, in comparisoun of Juda, brekere of the lawe.
Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
12 Go thou, and crye these wordis ayens the north; and thou schalt seie, Thou aduersarie, Israel, turne ayen, seith the Lord, and Y schal not turne awei my face fro you; for Y am hooli, seith the Lord, and Y schal not be wrooth with outen ende.
Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
13 Netheles knowe thou thi wickidnesse; for thou hast trespassid ayens thi Lord God, and thou hast spred abrood thi weies to aliens vndur ech tre ful of bowis; and thou herdist not my vois, seith the Lord.
Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
14 Be ye conuertid, sones, turnynge ayen, seith the Lord, for Y am youre hosebonde; and Y schal take you oon of a citee, and tweyne of a kynrede, and Y schal lede you in to Sion;
“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
15 and Y schal yyue to you scheepherdis after myn herte, and thei schulen feede you with kunnyng and teching.
Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
16 And whanne ye schulen be multiplied, and encreesse in the lond, in tho daies, seith the Lord, thei schulen no more seie, The arke of testament of the Lord; nether it schal stie on the herte, nether thei schulen thenke on it, nether it schal be visitid, nether it schal be ferthere.
Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
17 In that tyme thei schulen clepe Jerusalem The seete of the Lord, and alle hethene men schulen be gaderid togidere to it, in the name of the Lord, in Jerusalem; and thei schulen not go aftir the schrewidnesse of her worste herte.
Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
18 In tho daies the hous of Juda schal go to the hous of Israel; and thei schulen come togidere fro the lond of the north to the lond which Y yaf to youre fadris.
Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
19 Forsothe Y seide, Hou schal Y sette thee among sones, and schal yyue to thee a desirable lond, a ful cleer eritage of the oostis of hethene men? And Y seide, Thou schalt clepe me fadir, and thou schalt not ceesse to entre aftir me.
“Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 But as if a womman dispisith hir louyere, so the hous of Israel dispiside me, seith the Lord.
Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
21 A vois is herd in weies, the weping and yellyng of the sones of Israel; for thei maden wickid her weie, thei foryaten her Lord God.
Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
22 Be ye conuertid, sones, turnynge ayen, and Y schal heele youre turnyngis awei. Lo! we comen to thee; for thou art oure Lord God.
Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 Verili litil hillis weren lieris, the multitude of mounteyns was fals; verili in oure Lord God is the helthe of Israel.
Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 Schenschipe eete the trauel of oure fadris, fro oure yongthe; schenschipe eet the flockis of hem, and the droues of hem, the sones of hem, and the douytris of hem.
Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
25 We schulen slepe in oure schenschipe, and oure sclaundir schal hile vs; for we synneden to oure Lord God, bothe we and oure fadris, fro oure yongthe `til to this dai; and we herden not the vois of oure Lord God.
Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”

< Jeremiah 3 >