< Jeremiah 14 >

1 The word of the Lord, that was maad to Jeremye, of the wordis of dryenesse.
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 Jude weilide, and the yatis therof fellen doun, and ben maad derk in erthe, and the cry of Jerusalem stiede.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Grettere men senten her lesse men to water; thei camen to drawe watir, and thei foundun no water, thei brouyten ayen her vessels voide; thei weren schent and turmentid,
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 and thei hiliden her heedis for distriyng of the lond, for reyn cam not in the lond. Erthe tilieris weren schent, thei hiliden her heedis.
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 For whi and an hynde caluyde in the feeld, and lefte her calues, for noon eerbe was;
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 and wield assis stoden in rochis, and drowen wynde as dragouns; her iyen failiden, for noon eerbe was.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 If oure wickidnessis answeren to vs, Lord, do thou for thi name, for oure turnyngis awei ben manye; we han synned ayens thee.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Thou abidyng of Israel, the sauyour therof in the tyme of tribulacioun,
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 whi schalt thou be as a comelyng in the lond, and as a weigoere bowynge to dwelle? whi schalt thou be as a man of vnstable dwellyng, as a strong man that mai not saue? Forsothe, Lord, thou art in vs, and thin hooli name is clepid to help on vs; forsake thou not vs.
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 The Lord seith these thingis to this puple, that louede to stire hise feet, and restide not, and pleside not the Lord; now he schal haue mynde on the wickidnesses of hem, and he schal visite the synnes of hem.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 And the Lord seide to me, Nyle thou preie for this puple in to good.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 Whanne thei schulen faste, Y schal not here the preieris of hem; and if thei offren brent sacrifices and slayn sacrifices, Y schal not resseyue tho, for Y schal waste hem bi swerd and hungur and pestilence.
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 And Y seide, A! A! A! Lord God, profetis seien to hem, Ye schulen not se swerd, and hungur schal not be in you, but he schal yyue to you veri pees in this place.
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 And the Lord seide to me, The profetis profesien falsli in my name; Y sente not hem, and Y comaundide not to hem, nether Y spak to hem; thei profesien to you a fals reuelacioun, and a gileful dyuynyng, and the disseyuyng of her herte.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 Therfor the Lord seith these thingis of the profetis that profesien in my name, whiche Y sente not, and seien, Swerd and hungur schal not be in this lond; Tho profetis schulen be wastid bi swerd and hungur.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 And the puplis, to whiche thei profesieden, schulen be cast forth in the weies of Jerusalem, for hungur and swerd, and noon schal be, that schal birie hem; they and the wyues of hem, the sones and the douytris of hem `schulen be cast forth; and Y schal schede out on hem her yuel.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 And thou schalt seie to hem this word, Myn iyen lede doun a teer bi niyt and dai, and be not stille, for the virgyn, the douyter of my puple, is defoulid bi greet defoulying, with the worste wounde greetli.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 If Y go out to feeldis, lo! men ben slayn bi swerd; and if Y entre in to the citee, lo! men ben maad leene for hungur; also a profete and a prest yeden in to the lond which thei knewen not.
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Whether thou castynge awei hast cast awei Juda, ether thi soule hath wlatid Sion? whi therfor hast thou smyte vs, so that noon heelthe is? We abididen pees, and no good is; and we abididen time of heeling, and lo! disturbling is.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Lord, we han know oure vnfeithfulnessis, and the wickidnessis of oure fadris, for we han synned to thee.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Yyue thou not vs in to schenschip, for thi name, nether do thou dispite to vs; haue thou mynde on the seete of thi glorie, make thou not voide thi boond of pees with vs.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Whether in grauun ymagis of hethene men ben thei that reynen, ethir heuenes moun yyue reynes? whether thou art not oure Lord God, whom we abididen? For thou madist alle these thingis.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jeremiah 14 >