< Isaiah 57 >

1 A iust man perischith, and noon is, that thenkith in his herte; and men of merci ben gaderid togidere, for noon is that vndurstondith; for whi a iust man is gaderid fro the face of malice.
Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
2 Pees come, reste he in his bed, that yede in his dressyng.
Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 But ye, sones of the sekere of fals dyuynyng bi chiteryng of briddys, neiye hidur, the seed of auowtresse, and of an hoore.
“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 On whom scorneden ye? on whom maden ye greet the mouth, and puttiden out the tunge? Whethir ye ben not cursid sones, a seed of leesyngis?
Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
5 which ben coumfortid in goddis, vndur ech tree ful of bowis, and offren litle children in strondis, vndur hiye stoonys.
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Thi part is in the partis of the stronde, this is thi part; and to tho thou scheddist out moist offryng, thou offridist sacrifice. Whether Y schal not haue indignacioun on these thingis?
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Thou puttidist thi bed on an hiy hil and enhaunsid, and thidur thou stiedist to offre sacrifices;
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 and thou settidist thi memorial bihynde the dore, and bihynde the post. For bisidis me thou vnhilidist, and tokist auouter; thou alargidist thi bed, and madist a boond of pees with hem; thou louedist the bed of hem with openyd hond,
Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 and ournedist thee with kyngis oynement, and thou multipliedist thi pymentis; thou sentist fer thi messangeris, and thou art maad low `til to hellis. (Sheol h7585)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
10 Thou trauelidist in the multitude of thi weie, and seidist not, Y schal reste; thou hast founde the weie of thin hond,
Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 therfor thou preiedist not. For what thing dreddist thou bisy, for thou liedist, and thouytist not on me? And thou thouytist not in thin herte, that Y am stille, and as not seynge; and thou hast foryete me.
“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Y schal telle thi riytfulnesse, and thi werkis schulen not profite to thee.
Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Whanne thou schalt crie, thi gaderid tresours delyuere thee; and the wynd schal take awei alle tho, a blast schal do awei hem; but he that hath trist on me, schal enherite the lond, and schal haue in possessioun myn hooli hil.
Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
14 And Y schal seie, Make ye weie, yyue ye iurney, bowe ye fro the path, do ye awei hirtyngis fro the weie of my puple.
Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 For the Lord hiy, and enhaunsid, seith these thingis, that dwellith in euerlastyngnesse, and his hooli name in hiy place, and that dwellith in hooli, and with a contrite and meke spirit, that he quykene the spirit of meke men, and quykene the herte of contrit men.
Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 For Y schal not stryue with outen ende, nether Y schal be wrooth `til to the ende; for whi a spirit schal go out fro my face, and Y schal make blastis.
Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Y was wrooth for the wickidnesse of his aueryce, and Y smoot hym. Y hidde my face fro thee, and Y hadde indignacioun; and he yede with out stidfast dwellyng, in the weie of his herte.
Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Y siy hise weies, and Y helide hym, and Y brouyte hym ayen; and Y yaf coumfortyngis to hym, and to the moreneris of hym.
Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 Y made the fruyt of lippis pees, pees to hym that is fer, and to hym that is niy, seide the Lord; and Y heelide hym.
anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
20 But wickid men ben as the buyling see, that may not reste; and the wawis therof fleten ayen in to defoulyng, and fen.
Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 The Lord God seide, Pees is not to wickid men.
“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

< Isaiah 57 >