< Isaiah 39 >

1 In that tyme Marodach Baladan, the sone of Baladam, the kyng of Babiloyne, sente bookis and yiftis to Ezechie; for he hadde herd, that Ezechie hadde be sijk, and was rekyuerid.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Forsothe Ezechie was glad on hem, and schewide to hem the selle of swete smellynge spices, and of siluer, and of gold, and of smellynge thingis, and of best oynement, and alle the schoppis of his purtenaunce of houshold, and alle thingis that weren foundun in hise tresours; no word was, which Ezechie schewide not to hem in his hous, and in al his power.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Sotheli Ysaie, the prophete, entride to kyng Ezechie, and seide to hym, What seiden thes men, and fro whennus camen thei to thee? And Ezechie seide, Fro a fer lond thei camen to me, fro Babiloyne.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 And Ysaie seide, What siyen thei in thin hous? And Ezechie seide, Thei sien alle thingis that ben in myn hous; no thing was in my tresours, which Y schewide not to hem.
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 And Ysaie seide to Ezechie, Here thou the word of the Lord of oostis.
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Lo! daies schulen come, and alle thingis that ben in thin hous, and whiche thingis thi fadris tresoriden til to this dai, schulen be takun awei in to Babiloyne; not ony thing schal be left, seith the Lord.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 And thei schulen take of thi sones, that schulen go out of thee, whiche thou schalt gendre; and thei schulen be onest seruauntis and chast in the paleis of the kyng of Babiloyne.
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 And Ezechie seide to Ysaie, The word of the Lord is good, which he spak. And Ezechie seide, Pees and treuthe be maad oneli in my daies.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

< Isaiah 39 >