< Isaiah 27 >

1 In that dai the Lord schal visite in his hard swerd, and greet, and strong, on leuyathan, serpent, a barre, and on leuyathan, the crookid serpent; and he schal sle the whal, which is in the see.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 In that dai the vyner of cleen wyn and good schal synge to him.
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 Y am the Lord that kepe that vyner; sudeynli Y schal yyue drynke to it, lest perauenture it be visitid ayens it;
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 nyyt and dai Y kepe it, indignacioun is not to me. Who schal yyue me a thorn and brere? In batel Y schal go on it, Y schal brenne it togidere.
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Whether rathere Y schal holde my strengthe? It schal make pees to me, it schal make pees to me, for
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 the merit of hem that schulen go out with fersnesse fro Jacob. Israel schal floure and brynge forth seed, and thei schulen fille the face of the world with seed.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Whether he smoot it bi the wounde of the puple of Jewis smytynge hym? ether as it killide the slayn men of hym, so it was slayn?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 In mesure ayens mesure, whanne it schal be cast awei, he schal deme it; he bithouyte in his hard spirit, bi the dai of heete.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Therfor on this thing wickidnesse schal be foryouun to the hous of Jacob, and this schal be al the fruyt, that the synne therof be don awei, whanne it hath set all the stoonys of the auter as the stoonys of aische hurtlid doun. Wodis and templis schulen not stonde.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Forsothe the strong citee schal be desolat, the fair citee schal be left, and schal be forsakun as a desert; there a calf schal be lesewid, and schal ligge there, and schal waste the hiynessis therof.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 In the drynesse of ripe corn therof wymmen comynge, and thei that techen it, schulen be al to-brokun. Forsothe it is not a wijs puple, therfor he that made it, schal not haue mercy on it; and he that formyde it, schal not spare it.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 And it schal be, in that dai the Lord schal smyte thee, fro the botme of the flood `til to the stronde of Egipt; and ye sones of Israel, schulen be gaderid oon and oon.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 And it schal be, in that dai me schal come with a greet trumpe, and thei that weren lost, schulen come fro the lond of Assiriens, and thei that weren cast out, schulen come fro the lond of Egipt; and they schulen worschipe the Lord, in the hooli hil in Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

< Isaiah 27 >