< Isaiah 15 >

1 The birthun of Moab. For Ar was destried in niyt, Moab was stille; for the wal was distried in the niyt, Moab was stille.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 The kingis hous, and Dybon stieden to hiy places, in to weilyng; on Nabo, and on Medaba Moab schal yelle. In alle hedis therof schal be ballidnesse, and ech beerd schal be schauun.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 In the meetyng of thre weies therof thei ben gird in a sak, alle yellyng on the housis therof and in the stretis therof; it schal go doun in to wepyng.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 Esebon schal crie, and Eleale, the vois of hem is herd `til to Jasa; on this thing the redi men of Moab schulen yelle, the soule therof schal yelle to it silf.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Myn herte schal crie to Moab, the barris therof `til to Segor, a cow calf of thre yeer. For whi a wepere schal stie bi the stiyng of Luith, and in the weie of Oronaym thei schulen reise cry of sorewe.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 For whi the watris of Nemrym schulen be forsakun; for the eerbe dried up, buriownyng failide, al grenenesse perischide.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Bi the greetnesse of werk, and the visityng of hem, to the stronde of salewis thei schulen lede hem.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 For whi cry cumpasside the ende of Moab; `til to Galym the yellyng therof, and the cry therof `til to the pit of Helym.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 For the watris of Dibon ben fillid with blood; for Y schal sette encreessyngis on Dibon, to tho men of Moab that fledden fro the lioun, and to the relifs of the lond.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Isaiah 15 >