< Hosea 8 >

1 A trumpe be in thi throte, as an egle on the hous of the Lord; for that that thei yeden ouer my boond of pees, and braken my lawe.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Thei clepiden me to helpe, A! my God, we Israel han knowe thee.
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Israel hath cast awei good, the enemye schal pursue hym.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 Thei regnyden, and not of me; thei weren princes, and Y knew not. Thei maden her gold and siluer idols to hem, that thei schulden perische.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 A! Samarie, thi calf is cast awei; my strong veniaunce is wrooth ayens hem. Hou long moun thei not be clensid?
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 for also it is of Israel. A crafti man made it, and it is not god; for the calf of Samarie schal be in to webbis of ireyns.
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 For thei schulen sowe wynd, and thei schulen repe whirlewynd. A stalke stondynge is not in hem, the seed schal not make mele; that if also it makith mele, aliens schulen ete it.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Israel is deuouryd; now Israel is maad as an vnclene vessel among naciouns,
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 for thei stieden to Assur. Effraym is a wielde asse, solitarie to hym silf. Thei yauen yiftis to louyeris;
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 but also with meede thei hiriden naciouns. Now Y schal gadere hem togidere, and thei schulen reste a litil fro birthun of the kyng and of princes.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 For Efraym multipliede auteris to do synne, auteris weren maad to hym in to trespas.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Y schal write to hem my many fold lawis, that ben arettid as alien lawis.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Thei schulen brynge sacrifices, thei shulen offre, and ete fleischis; and the Lord schal not resseyue tho. Now he schal haue mynde on the wickidnessis of hem, and he schal visite the synnes of hem; thei schulen turne in to Egipt.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 And Israel foryat his makere, and bildide templis to idols, and Judas multipliede stronge citees; and Y schal sende fier in to the citees of hym, and it schal deuoure the housis of hym.
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”

< Hosea 8 >