< Genesis 8 >

1 Forsothe the Lord hadde mynde of Noe, and of alle lyuynge beestis, and of alle werk beestis, that weren with hym in the schip; and brouyte a wynd on the erthe.
Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
2 And watris weren decreessid, and the wellis of the see weren closid, and the wyndowis of heuene weren closid, and reynes of heuene weren ceessid.
Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
3 And watrys turneden ayen fro erthe, and yeden ayen, and bigunnen to be decreessid aftir an hundrid and fifti daies.
Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
4 And the schip restide in the seuenthe monthe, in the seuene and twentithe dai of the monthe, on the hillis of Armenye.
ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
5 And sotheli the watrys yeden and decresiden til to the tenthe monethe, for in the tenthe monethe, in the firste dai of the monethe, the coppis of hillis apperiden.
Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
6 And whanne fourti daies weren passid, Noe openyde the wyndow of the schip which he hadde maad, and sente out a crowe,
Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
7 which yede out, and turnede not ayen til the watris weren dried on erthe.
natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
8 Also Noe sente out a culuer aftir hym, to se if the watris hadden ceessid thanne on the face of erthe;
Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
9 and whanne the culuer foond not where hir foot schulde reste, sche turnede ayen to hym in to the schip, for the watris weren on al erthe; and Noe helde forth his hoond, and brouyte the culuer takun in to the schip.
Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
10 Sotheli whanne othere seuene daies weren abedun aftirward, eft he leet out a culuer fro the schip;
Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
11 and sche cam to hym at euentid, and bare in hir mouth a braunche of olyue tre with greene leeuys. Therfor Noe vndirstood that the watris hadden ceessid on erthe;
Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
12 and neuerthelesse he abood seuene othere daies, and sente out a culuer, which turnede `no more ayen to hym.
Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
13 Therfor in the sixe hundrid and o yeer of the lijf of Noe, in the firste monethe, in the firste day of the monethe, watris weren decreessid on erthe; and Noe openede the roof of the schip, and bihelde and seiy that the face of the erthe was dried.
Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
14 In the secunde monethe, in the seuene and twentithe dai of the monethe, the erthe was maad drie.
Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
15 Sotheli the Lord spak to Noe;
Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
16 and seide, Go out of the schip, thou, and thi wijf, thi sones, and the wyues of thi sones with thee;
“Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
17 and lede out with thee alle lyuynge beestis that ben at thee of ech fleisch, as wel in volatilis as in vnresonable beestis, and alle `reptils that crepen on erthe; and entre ye on the erthe, encreesse ye, and be ye multiplied on erthe.
Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
18 Therfor Noe yede out, and hise sones, and his wijf, and the wyues of hise sones with hym;
Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
19 but also alle lyuynge beestis, and werk beestis, and `reptils that crepen on erthe, bi her kynde, yeden out of the schip.
Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
20 Forsothe Noe bildide an auter to the Lord, and he took of alle clene beestis and briddis, and offride brent sacrifices on the auter.
Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
21 And the Lord sauerede the odour of swetnesse, and seide to hym, Y schal no more curse the erthe for men, for the wit and thouyt of mannus herte ben redi in to yuel fro yong wexynge age; therfor Y schal no more smyte ech lyuynge soule as Y dide;
Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
22 in alle the daies of erthe, seed and ripe corn, coold and heete, somer and wyntir, nyyt and dai, shulen not reste.
“Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark