< Genesis 4 >

1 Forsothe Adam knewe Eue his wijf, which conseyuede, and childide Cayn, and seide, Y haue gete a man bi God.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 And efte sche childide his brother Abel. Forsothe Abel was a kepere of scheep, and Cayn was an erthe tilyere.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Sotheli it was don after many daies, that Cayn offride yiftis to the Lord of the fruytis of erthe;
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 and Abel offride of the first gendrid of his floc, and of the fatnesse of tho. And the Lord bihelde to Abel and to the yiftis of hym;
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 sotheli he bihelde not to Cayn and to hise yiftis. And Cayn was wrooth greetli, and his cheer felde doun.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 And the Lord seide to hym, Whi art thou wrooth, and whi felde doun thi face?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Whether not if thou schalt do wel, thou schalt resseyue; but if thou doist yuele, thi synne schal be present anoon in the yatis? but the desir therof schal be vndur thee, and thou schalt be lord therof.
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 And Cayn seide to Abel his brother, Go we out. And whanne thei weren in the feeld, Cayn roos ayens his brother Abel, and killide him.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 And the Lord seide to Cayn, Where is Abel thi brother? Which answerde, Y woot not; whether Y am the kepere of my brothir?
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 And God seide to Cayn, What hast thou do? the vois of the blood of thi brother crieth to me fro erthe.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Now therfor thou schalt be cursid on erthe, that openyde his mouth, and resseyuede of thin hond the blood of thi brothir.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Whanne thou schalt worche the erthe, it schal not yyue his fruytis to thee; thou schalt be vnstable of dwellyng and fleynge aboute on erthe in alle the daies of thi lijf.
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 And Cayn seide to the Lord, My wickidnesse is more than that Y disserue foryyuenesse; lo!
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 to dai thou castist me out fro the face of the erthe; and Y schal be hid fro thi face, and Y schal be vnstable of dwellyng and fleynge aboute in erthe; therfore ech man that schal fynde me schal slee me.
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 And the Lord seide to hym, It schal not be don so, but ech man that schal slee Cayn shal be punyschid seuenfold. And the Lord settide a signe in Cayn, that ech man that schulde fynde hym schulde not slee hym.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 And Cayn yede out fro the face of the Lord, and dwellide fleynge aboute in erthe, at the eest coost of Eden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Forsothe Cayn knewe his wiif, which conseyuede, and childide Enoth; and Cayn bildide a citee, and clepide the name therof of the name of hise sone Enoth.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Forsothe Enoth gendride Irad, and Irad gendride Manyael, and Manyael gendride Matusael, and Matusael gendride Lameth;
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 that took twei wyues, the name to o wijf was Ada, and the name to the tother was Sella.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 And Ada gendride Jabel, that was the fadir of dwellers in tentis and of shepherdis;
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 and the name of his brother was Tubal, he was the fadir of syngeris in harpe and orgun.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 And Sella gendride Tubalcayn, that was an hamerbetere, and smyyt on alle werkis of bras and of yrun; forsothe the sistir of Tubalcayn was Neoma.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 And Lameth seide to his wyues Ada and Sella, Ye wyues of Lameth, here my vois, and herkne my word; for Y haue slayn a man bi my wounde, and a yong wexynge man bi my `violent betyng;
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 veniaunce schal be youun seuenfold of Cayn, forsothe of Lameth seuentisithis seuensithis.
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Also yit Adam knewe his wijf, and sche childide a sone, and clepide his name Seth, and seide, God hath put to me another seed for Abel, whom Cayn killide.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 But also a sone was borun to Seth, which sone he clepide Enos; this Enos bigan to clepe inwardli the name of the Lord.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Genesis 4 >