< Genesis 39 >

1 Therfor Joseph was led in to Egipt, and Putifar, `chast and onest seruaunt of Farao, prince of the oost, a man of Egipt, bouyte hym of the hondis of Ismaelitis, of which he was brouyt.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 And the Lord was with hym, and he was a man doynge with prosperite in alle thingis. And Joseph dwellide in `the hows of his lord,
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 which knew best that the Lord was with Joseph, and that alle thingis whiche he dide, weren dressid of the Lord in `the hond of hym.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 And Joseph foond grace bifor his lord, and `mynystride to hym, of whom Joseph was maad souereyn of alle thingis, and gouernede the hows bitaken to hym, and alle thingis that weren bitakun to hym.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 And the Lord blesside the `hows of Egipcian for Joseph, and multipliede al his catel, as wel in howsis as in feeldis;
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 nether he knew ony other thing no but `breed which he eet. Forsothe Joseph was fair in face, and schapli in siyt.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 And so aftir many daies the ladi castide hir iyen in to Joseph, and seide, Slepe thou with me;
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 which assentide not to the vnleueful werk, and seide to hir, Lo! while alle thingis ben bitakun to me, my lord woot not what he hath in his hows,
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 nether ony thing is, which is not in my power, ether which `he hath not bitake to me, outakun thee, which art his wijf; how therfor may Y do this yuel, and do synne ayens my lord?
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Thei spaken siche wordis `bi alle daies, and the womman was diseseful to the yong waxynge man, and he forsook auoutrie.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Forsothe it bifelde in a dai, that Joseph entride in to the hows, and dide sum werk with out witnessis.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 And sche took `the hem of his clooth, and sche seide, Slepe thou with me; and he lefte the mentil in hir hoond, and he fledde, and yede out.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 And whanne the womman hadde seyn the clooth in hir hondis, and that sche was dispisid,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 sche clepide to hir the men of hir hows, and seide to hem, Lo! my lord hath brouyt in an Ebrew man, that he schulde scorn vs; he entride to me to do leccherie with me, and whanne Y criede, and he herde my vois,
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 he lefte the mentil which Y helde, and he fledde out.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Therfor in to the preuyng of trouthe, sche schewide the mantil, holdun to the hosebonde turnynge ayen hoom.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 And she seide, The Ebrew seruaunt, whom thou brouytist, entride to me to scorne me; and whanne he siy me crye,
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 he lefte the mentil which Y helde, and he fledde out.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 And whanne these thingis weren herd, the lord bileuyde ouer myche to the wordis of the wijf, and was ful wrooth;
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 and he bitook Joseph in to prisoun, where the bounden men of the kyng weren kept, and he was closid there.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Forsothe the Lord was with Joseph, and hadde mercy on hym, and yaf grace to hym in the siyt of the prince of the prisoun,
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 which bitook in the hond of Joseph alle prisoneris that weren holdun in kepyng, and what euer thing was doon, it was vndur Joseph, nethir the prince knewe ony thing,
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 for alle thingis weren bitakun to Joseph; for the Lord was with hym, and dresside alle his werkis.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Genesis 39 >