< Genesis 35 >

1 Yn the mene tyme the Lord spak to Jacob, Ryse thou, and stie to Bethel, and dwelle thou there, and make thou an auter to the Lord, that apperide to thee whanne thou fleddist Esau, thi brother.
Tsono Mulungu anati kwa Yakobo, “Nyamuka uchoke kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ukamange guwa lansembe la Mulungu amene anadza kwa iwe pamene umathawa Esau, mʼbale wako.”
2 Forsothe Jacob seide, whanne al his hous was clepid to gidere, Caste ye a wei alien goddis, that ben `in the myddis of you, and be ye clensid, and chaunge ye youre clothis;
Choncho Yakobo anawuza a pa banja pake ndi onse amene anali naye kuti, “Chotsani milungu yachilendo imene muli nayo, ndipo mudziyeretse nokha ndi kusintha zovala zanu.
3 rise ye, and stie we into Bethel, that we make there an auter to the Lord, which herde me in the dai of my tribulacioun, and was felowe of my weie.
Tiyeni tinyamuke kuchoka kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ndikamumangira guwa lansembe Mulungu amene anandithandiza pa nthawi za masautso anga, komanso amene wakhala nane mʼmayendedwe anga onse.”
4 Therfor thei yauen to hym alle alien goddis which thei hadden, and eere ryngis, that weren in `the eeris of hem; and he deluyde tho vndur a `tre, clepid therubynte, which is bihynde the citee of Sichem.
Choncho anamupatsa Yakobo milungu yachilendo yonse imene anali nayo pamodzi ndi ndolo. Iye anazikwirira pansi pa mtengo wa thundu ku Sekemu.
5 And whanne thei yeden, drede assailide alle men by cumpas of the citee, and thei weren not hardi to pursue hem goynge a wei.
Pamenepo ananyamuka, ndipo mtima woopa Mulungu unagwera anthu onse a mʼmizinda yozungulira, kotero kuti palibe aliyense amene anatsatira banja la Yakobo.
6 Therfor Jacob cam to Lusa, which is in the lond of Canaan, bi `sire name Bethel, he and al his puple with hym.
Yakobo ndi anthu onse anali naye aja anafika ku Luzi (ku Beteli) mu dziko la Kanaani.
7 And he bildide there an auter to the Lord, and clepide the name of that place The hows of God, for God apperide there to hym, whanne he fledde his brothir.
Kumeneko anamanga guwa lansembe nalitcha Eli Beteli, chifukwa kunali kumeneko kumene Mulungu anadziwulula yekha kwa Yakobo pamene ankathawa mʼbale wake.
8 Delbora, the nurische of Rebecca, diede in the same tyme, and sche was biried at the roote of Bethel, vndir an ook, and the name of the place was clepid The ook of wepyng.
Debora mlezi wa Rakele anamwalira komweko nayikidwa mʼmanda pansi pa mtengo wa thundu cha kumunsi kwa Beteli. Choncho panatchedwa Aloni-Bakuti (mtengo wamaliro).
9 Forsothe God apperide eft to Jacob, aftir that he turnede ayen fro Mesopotanye of Sirie, and cam into Bethel, and blesside hym,
Yakobo atabwera kuchokera ku Padanaramu, Mulungu anabweranso kwa iye namudalitsa.
10 and seide, Thou schalt no more be clepid Jacob, but Israel schal be thi name. And God clepide hym Israel, and seide to hym,
Mulungu anati kwa iye, “Dzina lako ndiwe Yakobo, koma sudzatchedwanso Yakobo; koma udzatchedwa Israeli.” Choncho anamutcha iye Israeli.
11 Y am God Almyyti, encreesse thou, and be thou multiplied, folkis and puplis of naciouns schulen be of thee, kyngis schulen go out of thi leendis;
Ndipo Mulungu anati kwa iye, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse; berekanani ndi kuchulukana. Mtundu wa anthu, inde, mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe, ndipo ena mwa zidzukulu zako adzakhala mafumu.
12 and Y shal yyue to thee, and to thi seed after thee, the lond which Y yaf to Abraham, and Ysaac.
Dziko limene ndinapereka kwa Abrahamu ndi Isake ndiliperekanso kwa iwe. Lidzakhala lako ndi la zidzukulu zako.”
13 And God departide fro hym.
Kenaka Mulungu anamusiya Yakobo.
14 Forsothe Jacob reiside a title ether memorial of stoonys, in the place where ynne God spak to hym, and he sacrifiede ther onne fletynge sacrifices, and schedde out oile,
Yakobo anayika mwala wachikumbutso pa malo pamene Mulungu anayankhula naye paja. Iye anathirapo nsembe yachakumwa ndi yamafuta.
15 and clepide the name of that place Bethel.
Yakobo anawatcha malo amene Mulungu anayankhula naye aja kuti Beteli.
16 Forsothe Jacob yede out fro thennus, and cam in the bigynnynge of somer to the lond that ledith to Effrata; in which lond whanne Rachel trauelide in child beryng,
Kenaka anachoka ku Beteli. Koma ali pafupi kufika ku Efurata nthawi yakuti Rakele aone mwana inakwana. Iye anavutika pobereka.
17 sche bigan to be in perel for the hardnesse of childberyng; and the medewijf seide to hir, Nyle thou drede, for thou schalt haue also this sone.
Akanali chivutikire choncho, mzamba anamulimbikitsa nati, “Usaope pakuti ubala mwana wina wamwamuna.”
18 Forsothe while the soule yede out for sorew, and deeth neiyede thanne, she clepide the name of hir sone Bennony, that is, the sone of my sorewe; forsothe the fadir clepide hym Beniamyn, that is the sone of the riyt side.
Tsono pamene Rakele ankapuma wefuwefu (popeza ankamwalira) iye anatcha mwana uja kuti Beni-Oni. Koma abambo ake anamutcha kuti Benjamini.
19 Therfor Rachel diede, and was biriede in the weie that ledith to Effrata, this is Bethleem.
Choncho Rakele anamwalira ndipo anayikidwa pa njira yopita ku Efurata (Kumeneko ndiye ku Betelehemu).
20 And Jacob bildide a title on the sepulcre of hir; this is the title of biriel of Rachel `til into present dai.
Pa manda ake, Yakobo anayimika mwala wachikumbutso wa pa manda ndipo ulipobe mpaka lero.
21 Jacob yede fro thennus, and settide tabernacle ouer the tour of the flok.
Israeli (Yakobo) anasunthanso nakamanga tenti yake kupitirira nsanja ya Ederi.
22 And while he dwellide in that cuntrei, Ruben yede, and slepte with Bala, the secundarie wijf of his fadir, which thing was not hid fro hym. Forsothe the sones of Jacob weren twelue;
Israeli akanali mʼderali, Rubeni anapita nakagonana ndi Biliha, mdzakazi wa abambo ake. Yakobo uja anazimva zimenezi. Yakobo anali ndi ana aamuna khumi ndi awiri:
23 the sones of Lia weren, the firste gendrid Ruben, and Symeon, and Leuy, and Judas, and Isachar, and Zabulon;
Ana a Leya ndi awa: Rubeni anali mwana woyamba wa Yakobo, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, ndi Zebuloni.
24 the sones of Rachel weren, Joseph and Beniamyn;
Ana a Rakele ndi awa: Yosefe ndi Benjamini.
25 the sones of Bala, handmayde of Rachel, weren Dan, and Neptalym;
Ana a Biliha, wantchito wa Rakele ndi awa: Dani ndi Nafutali.
26 the sones of Zelfa, handmayde of Lya, weren Gad, and Aser. These weren the sones of Jacob, that weren borun to hym in Mesopotanye of Sirie.
Ana a Zilipa wantchito wa Leya ndi awa: Gadi ndi Aseri. Awa ndiwo ana a Yakobo amene anabadwira ku Padanaramu.
27 Also Jacob came to Isaac, his fadir, in to Manbre, a citee Arabee, this is Ebron, in which Manbre Abraham `and Isaac was a pylgrym.
Yakobo anafika ku mudzi kwa abambo ake Isake ku Mamre, (kumene kunkatchedwa ku Kiriyati-Ariba kapenanso Hebroni) kumene Abrahamu ndi Isake anakhalako kale.
28 And the daies of Isaac weren fillid an hundrid and foure scoore of yeris;
Isake anakhala ndi moyo zaka 180.
29 and he was wastid in age, and diede, and he was put to his puple, and was eeld, and ful of daies; and Esau and Jacob his sones birieden hym.
Anamwalira ali wokalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ndipo ana ake Esau ndi Yakobo anamuyika mʼmanda.

< Genesis 35 >