< Genesis 21 >

1 Forsothe God visitide Sare, as he bihiyte, and fillide tho thingis, that he spak.
Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
2 And sche conseyuede, and childide a sone in hir eeld, in the tyme wherynne God biforseide to hir.
Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
3 And Abraham clepide the name of his sone, whom Sare childide to him, Ysaac.
Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
4 And Abraham circumcidide hym in the eiyte dai, as God comaundide to him,
Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
5 whanne he was of an hundrid yeer; for Ysaac was borun in this age of the fadir.
Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
6 And Sare seide, The Lord made leiyynge to me, and who euer schal here schal leiye with me.
Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
7 And eft sche seide, Who schulde here, and bileue to Abraham, that Sare schulde yyue soukyng to a sone, whom sche childide to him now an eld man?
Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
8 Therfor the child encreesside, and was wenyd; and Abraham made a greet feeste in the dai of his wenyng.
Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
9 And whanne Sare seiy the sone of Agar Egipcian pleiynge with Ysaac hir sone, sche seide to Abraham,
Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
10 Cast thou out the handmayde and hir sone; for the sone of the handmayde schal not be eir with my sone Ysaac.
ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
11 Abraham took this heuyli for his sone;
Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
12 and God seide to hym, Be it not seyn scharp to thee on the child, and on thin handmayde; alle thingis whiche Sare seith to thee, here thou hir vois, for in Isaac seed schal be clepid to thee;
Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
13 but also I schal make the sone of the handmaid in to a greet folk, for he is thi seed.
Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
14 And so Abraham roos eerli, and took breed, and a botel of watir, and puttide on hir schuldre, and bitook the child, and lefte hir; and whanne sche hadde go, sche yede out of the weie in the wildirnesse of Bersabee.
Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
15 And whanne the watir in the botel was endid, sche castide awei the child vndur a tre that was there;
Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
16 and sche yede awei, and sche sat euene ayens as fer as a bowe may caste; for sche seide, Y schal not se the child diynge; and sche sat ayens, and reiside hir vois, and wepte.
Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
17 Forsothe the Lord herde the vois of the child, and the aungel of the Lord clepide Agar fro heuene, and seide, What doist thou, Agar? nyle thou drede, for God hath herd the vois of the child fro the place where ynne he is.
Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
18 Rise thou, and take the child, and holde his hoond; for Y schal make hym in to a greet folc.
Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
19 And God openyde hir iyen, and sche seiy a pit of watir, and sche yede, and fillide the botel, and sche yaf drynk to the child;
Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
20 and was with him, and he encresside, and dwellide in wildernesse, and he was maad a yong man an archer,
Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
21 and dwellide in the deseert of Faran; and his modir took to him a wijf of the lond of Egipt.
Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
22 In the same tyme Abymelech, and Ficol, prince of his oost, seide to Abraham, God is with thee in alle thingis whiche thou doist;
Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
23 therfore swere thou bi God that thou noye not me, and myn eiris, and my kynrede; but bi the mersi whych Y dide to thee, do thou to me, and to the lond in which thou lyuedist a comelyng.
Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
24 And Abraham seide, Y schal swere.
Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
25 And he blamyde Abymelech for the pit of watir, which hise seruauntis token awey bi violence.
Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
26 And Abymelech answerde, I wiste not who dide this thing, but also thou schewidist not to me, and Y herde not outakun to dai.
Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
27 And so Abraham took scheep and oxun, and yaf to Abymalech, and bothe smyten a boond of pees.
Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
28 And Abraham settide seuene ewe lambren of the flok asidis half.
Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
29 And Abymelech seide to hym, What wolen these seuene ewe lambren to hem silf, whiche thou madist stonde asidis half?
ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
30 And he seide, Thou schalt take of myn hond seuene ewe lambren, that tho be in to witnessyng to me, for Y diggide this pit.
Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
31 Therfor thilke place was clepid Bersabee, for euere eithir swore there;
Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
32 and thei maden boond of pees for the pit of an ooth.
Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
33 Forsothe Abymelech roos, and Ficol, prince of his chyualrie, and thei turneden ayen in to the lond of Palestyns. Sotheli Abraham plauntide a wode in Bersabee, and inwardli clepide there the name of euerlastinge God;
Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
34 and he was an erthetiliere ether a comelynge of the lond of Palestynes in many dayes.
Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

< Genesis 21 >