< Genesis 18 >

1 Forsothe in the valei of Mambre the Lord apperide to Abraham, sittynge in the dore of his tabernacle, in thilke heete of the dai.
Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
2 And whanne he hadde reisid his iyen, thre men apperiden to hym, and stoden nyy hym. And whanne he hadde seyn hem, he ran fro the dore of his tabernacle in to the meting of hem, and he worschipide on erthe,
Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
3 and seide, Lord, if Y haue founde grace in thin iyen, passe thou not thi seruaunt,
“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
4 but I schal brynge a litil watir, and youre feet be waischid, and reste ye vndur the tre;
Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
5 and Y schal sette a mussel of breed, and youre herte be coumfortid; aftirward ye schulen passe; for herfor ye bowiden to youre seruaunt. Whiche seiden, Do thou as thou hast spoke.
Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
6 Abraham hastide in to the tabernacle, to Sare, and seide to hir, Hast thou, meddle thou thre half buschelis of clene flour; and make thou looues bakun vndur aischis.
Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
7 Forsothe he ran to the droue of beestis, and took therof a calf moost tendre and best, and yaf to a child, which hastide, and sethede the calfe;
Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
8 and he took botere, and mylk, and the calf which he hadde sode, and settide bifore hem; forsothe Abraham stood bisidis hem vndur the tre.
Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
9 And whanne thei hadden ete, thei seiden to hym, Where is Sare thi wijf? He answerde, Lo! sche is in the tabernacle.
Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
10 To whom the Lord seide, Y schal turne ayen, and Y schal come to thee in this tyme, if Y lyue; and Sare, thi wijf, schal haue a sone. Whanne this was herd, Sare leiyede bihynde the dore of the tabernacle.
Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
11 Forsothe bothe weren olde, and of greet age, and wommans termes ceessiden to be maad to Sare.
Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
12 And she leiyede, seiynge pryueli, after that Y wexede eld, and my lord is eld, schal Y yyue diligence to lust?
Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
13 Forsothe the Lord seide to Abraham, Whi leiyeth Sare, thi wijf, seiynge, whether Y an eld womman schal bere child verili?
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
14 whether ony thing is hard to God? Bi the biheeste Y schal turne ayen to thee in this same tyme, if Y lyue; and Sara schal haue a sone.
Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
15 Sare was aferd for drede, and denyede, seiynge, Y leiyede not. Forsothe the Lord seide, It is not so, but thou leiyedist.
Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
16 Therfor whanne the men hadden risen fro thennus, thei dressiden the iyen ayens Sodom; and Abraham yede to gidre, ledynge hem forth.
Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
17 And the Lord seide, Wher Y mowe hele fro Abraham what thingis Y schal do,
Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
18 sithen he schal be in to a greet folk and moost strong, and alle naciouns of erthe schulen be blessid in hym?
Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
19 For Y woot that Abraham schal comaunde hise children, and his hows after hym, that thei kepe the weie of the Lord, and that thei do riytfulnesse and dom, that the Lord bringe for Abraham alle thingis whiche he spak to Abraham.
Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
20 And so the Lord seide, The cry of men of Sodom and of men of Gomorre is multiplied, and her synne is agreggid greetli; Y schal come doun,
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
21 and schal se whether thei han fillid in werk the cry that cam to me, that Y wite whether it is not so.
choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
22 And thei turneden han fro thennus, and yeden to Sodom. Abraham sotheli stood yit bifore the Lord,
Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
23 and neiyede, and seide, Whether thou schalt leese a iust man with the wickid man?
Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
24 if fifti iust men ben in the citee, schulen thei perische togidere, and schalt thou not spare that place for fifti iust men, if thei ben ther ynne?
Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
25 Fer be it fro thee that thou do this thing, and sle a iust man with a wickid man, and that a iust man be maad as a wickid man; this is not thin that demest al erthe; thou schalt not make this doom.
Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
26 And the Lord seide to him, If Y schal fynde in Sodom fifti iust men in the myddis of the citee, Y schal foryyue to al the place for hem.
Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
27 Abraham answerde and seide, For Y bigan onys, Y schal speke to my Lord, sithen Y am dust and aische;
Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
28 what if lesse than fifti iust men bi fyue ben, schalt thou do a wey al the cite for fyue and fourti? And the Lord seide, Y schal not do a wei, if I schal fynde fyue and fourti there.
bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
29 And eft Abraham seide to hym, But if fourti ben there, what schalt thou do? The Lord seide, Y schal not smyte for fourti.
Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
30 Abraham seide, Lord, Y biseche, take thou not to indignacioun, if Y speke; what if thretti be foundun there? The Lord answerde, Y schal not do, if Y schal fynde thretti there.
Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
31 Abraham seide, For Y bigan onys, Y schal speke to my Lord; what if twenti be foundun there? The Lord seide, Y schal not sle for twenti.
Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
32 Abraham seide, Lord, Y biseche, be thou not wrooth, if Y speke yit onys; what if ten be founden there? The Lord seide, Y schal not do a wey for ten.
Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
33 The Lord yede forth, after that he ceesside to speke to Abraham, and Abraham turnede ayen in to his place.
Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

< Genesis 18 >