+ Genesis 1 >

1 In the bigynnyng God made of nouyt heuene and erthe.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 Forsothe the erthe was idel and voide, and derknessis weren on the face of depthe; and the Spiryt of the Lord was borun on the watris.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 And God seide, Liyt be maad, and liyt was maad.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 And God seiy the liyt, that it was good, and he departide the liyt fro derknessis,
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 and he clepide the liyt, dai, and the derknessis, nyyt. And the euentid and morwetid was maad, o daie.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 And God seide, The firmament be maad in the myddis of watris, and departe watris fro watris.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 And God made the firmament, and departide the watris that weren vndur the firmament fro these watris that weren on the firmament; and it was don so.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 And God clepide the firmament, heuene. And the euentid and morwetid was maad, the secounde dai.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 Forsothe God seide, The watris, that ben vndur heuene, be gaderid in to o place, and a drie place appere; and it was doon so.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 And God clepide the drie place, erthe; and he clepide the gadryngis togidere of watris, the sees. And God seiy that it was good;
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 and seide, The erthe brynge forth greene eerbe and makynge seed, and appil tre makynge fruyt bi his kynde, whos seed be in it silf on erthe; and it was doon so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 And the erthe brouyte forth greene erbe and makynge seed bi his kynde, and a tre makynge fruyt, and ech hauynge seed by his kynde. And God seiy that it was good.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 And the euentid and morwetid was maad, the thridde dai.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 Forsothe God seide, Liytis be maad in the firmament of heuene, and departe tho the dai and niyt; and be tho in to signes, and tymes, and daies, and yeeris;
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 and shyne tho in the firmament of heuene, and liytne tho the erthe; and it was doon so.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 And God made twei grete liytis, the gretter liyt that it schulde be bifore to the dai, and the lesse liyt that it schulde be bifore to the niyt;
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 and God made sterris; and settide tho in the firmament of heuene, that tho schulden schyne on erthe,
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 and that tho schulden be bifore to the dai and nyyt, and schulden departe liyt and derknesse. And God seiy that it was good.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 And the euentid and the morwetid was maad, the fourthe dai.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 Also God seide, The watris brynge forth a `crepynge beeste of lyuynge soule, and a brid fleynge aboue erthe vndur the firmament of heuene.
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 And God made of nouyt grete whallis, and ech lyuynge soule and mouable, whiche the watris han brouyt forth in to her kyndis; and God made of nouyt ech volatile bi his kynde. And God seiy that it was good;
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 and blesside hem, and seide, Wexe ye, and be ye multiplied, and fille ye the watris of the see, and briddis be multiplied on erthe.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 And the euentid and the morwetid was maad, the fyuethe dai.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 And God seide, The erthe brynge forth a lyuynge soul in his kynde, werk beestis, and `crepynge beestis, and vnresonable beestis of erthe, bi her kyndis; and it was don so.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 And God made vnresonable beestis of erthe bi her kyndes, and werk beestis, `and ech crepynge beeste of erthe in his kynde. And God seiy that it was good; and seide,
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 Make we man to oure ymage and liknesse, and be he souereyn to the fischis of the see, and to the volatilis of heuene, and to vnresonable beestis of erthe, and to ech creature, and to ech `crepynge beest, which is moued in erthe.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 And God made of nouyt a man to his ymage and liknesse; God made of nouyt a man, to the ymage of God; God made of nouyt hem, male and female.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 And God blesside hem, and seide, Encreesse ye, and be ye multiplied, and fille ye the erthe, and make ye it suget, and be ye lordis to fischis of the see, and to volatilis of heuene, and to alle lyuynge beestis that ben moued on erthe.
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 And God seide, Lo! Y haue youe to you ech eerbe berynge seed on erthe, and alle trees that han in hem silf the seed of her kynde, that tho be in to mete to you;
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 and to alle lyuynge beestis of erthe, and to ech brid of heuene, and to alle thingis that ben moued in erthe, and in whiche is a lyuynge soule, that tho haue to ete; and it was doon so.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 And God seiy alle thingis whiche he made, and tho weren ful goode. And the euentid and morwetid was maad, the sixte day.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

+ Genesis 1 >