< Ezekiel 46 >

1 The Lord God seith these thingis, The yate of the ynnere halle, that biholdith to the eest, schal be closid bi sixe daies, in whiche werk is doon; for it schal be openid in the dai of sabat, but also it schal be openyd in the dai of kalendis.
“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
2 And the prince schal entre bi the weie of the porche of the yate withoutforth, and he schal stonde in the threisfold of the yate; and preestis schulen make the brent sacrifice of hym, and the pesible sacrifices of hym; and he schal worschipe on the threisfold of the yate, and he schal go out; forsothe the yate schal not be closid til to the euentid.
Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
3 And the puple of the lond schal worschipe at the dore of that yate, in sabatis, and in calendis, bifor the Lord.
Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
4 Forsothe the prince schal offre this brent sacrifice to the Lord in the dai of sabat, sixe lambren with out wem, and a wether with out wem,
Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
5 and the sacrifice of ephi bi a wether; but in the lambren he schal offre the sacrifice which his hond schal yiue, and of oile the mesure hyn, bi ech ephi.
Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
6 But in the dai of calendis he schal offre a calf with out wem of the droue; and sixe lambren, and wetheris schulen be with out wem,
Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
7 and ephi bi a calf. Also he schal make the sacrifice ephi bi a wether; but of lambren as his hond fyndith, and of oile the mesure hyn, bi ech ephi.
Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
8 And whanne the prince schal entre, entre he bi the weie of the porche of the yate, and go he out bi the same weie.
Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
9 And whanne the puple of the lond schal entre in the siyt of the Lord, in solempnytees, which puple entrith bi the yate of the north, for to worschipe, go it out bi the wei of the south yate. Certis the puple that entrith bi the weie of the south yate, go out bi the weie of the north yate. It schal not turne ayen bi the weie of the yate, bi which it entride, but euene ayens that weie it schal go out.
“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
10 Forsothe the prince schal be in the myddis of hem; he schal entre with hem that entren, and he schal go out with hem that goen out.
Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
11 And in feiris and in solempnytees, the sacrifice of ephi schal be bi a calf, and ephi bi a wether; in lambren schal be sacrifice as his hond fyndith, and of oile the mesure hyn, bi ech ephi.
“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
12 Forsothe whanne the prince makith a wilful brent sacrifice, ether wilful pesible sacrifice to the Lord, the yate that biholdith to the eest, schal be openyd to hym; and he schal make his brent sacrifice, and hise pesible sacrifices, as it is wont to be doon in the dai of sabat; and he schal go out, and the yate schal be closid after that he yede out.
Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
13 And he schal make brent sacrifice ech day to the Lord, a lomb with out wem of the same yeer; euere he schal make it in the morewtid,
“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
14 and he schal make sacrifice on it ful eerli; eerli he schal make the sixte part of ephi, and of oile the thridde part of hyn, that it be meddlid with the floure of wheete; it is a lawful sacrifice, contynuel and euerlastinge, to the Lord.
Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
15 He schal make a lomb, and sacrifice, and oile, ful eerli; he schal make eerli brent sacrifice euerlastynge.
Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
16 The Lord God seith these thingis, If the prince yyueth an hous to ony of hise sones, the eritage of hym schal be of hise sones; thei schulen welde it bi eritage.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
17 Forsothe if he yyueth a biquest of his eritage to oon of hise seruauntis, it schal be his `til to the yeer of remyssioun, and it schal turne ayen to the prince; forsothe the eritage of hym schal be to hise sones.
Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
18 And the prince schal not take bi violence of the eritage of the puple, and of the possessioun of hem; but of his owne possessioun he schal yyue eritage to hise sones, that my puple be not scaterid, ech man fro his possessioun.
Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
19 And he ledde me in bi the entryng, that was on the side of the yate, in to the treseries of the seyntuarie to the preestis, whiche treseries bihelden to the north; and there was a place goynge to the west.
Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
20 And he seide to me, This is the place where prestis schulen sethe, bothe for synne and for trespas; where thei schulen sethe sacrifice, that thei bere not out in to the outermere halle, and the puple be halewid.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
21 And he ledde me out in to the outermere halle, and ledde me aboute bi the foure corneris of the halle; and lo! a litil halle was in the corner of the halle, alle litil hallis bi the corneris of the halle;
Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
22 in foure corneris of the halle litle hallis weren disposid, of fourti cubitis bi lengthe, and of thretti bi breede;
Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
23 foure weren of o mesure; and a wal bi cumpas yede aboute foure litle hallis; and kychenes weren maad vndur the porchis bi cumpas.
Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
24 And he seide to me, This is the hous of kichenes, in which the mynystris of the hous of the Lord schulen sethe the sacrifices of the puple.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

< Ezekiel 46 >