< Ezekiel 4 >

1 And thou, sone of man, take to thee a tijl stoon; and thou schalt sette it bifore thee, and thou schalt discriue ther ynne the citee of Jerusalem.
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 And thou schalt ordeyne bisegyng ayenus that Jerusalem; and thou schalt bilde strengthis, and thou schalt bere togidere erthe, and thou shalt yyue oostis of batel ayens it, and thou schalt sette engynes in cumpas.
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 And take thou to thee an irone friynge panne; and thou schalt sette it in to an irone wal bitwixe thee and bitwixe the cite; and thou schalt sette stidfastli thi face to it, and it schal be in to bisegyng, and thou schalt cumpasse it; it is a signe to the hous of Israel.
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 And thou schalt slepe on thi left side, and thou schalt putte the wickidnessis of the hous of Israel on that side, in the noumbre of daies in which thou shalt slepe on that side, and thou schalt take the wickidnesse of hem.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5 Forsothe Y yaf to thee the yeeris of the wickidnesse of hem bi noumbre of daies, thre hundrid and nynti daies; and thou schalt bere the wickidnesse of the hous of Israel.
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 And whanne thou hast fillid these thingis, thou schalt slepe the secounde tyme on thi riytside. And thou schalt take the wickidnesse of the hous of Juda bi fourti daies; Y yaf to thee a dai for a yeer, a dai sotheli for a yeer.
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 And thou schalt turne thi face to the biseging of Jerusalem; and thin arm schal be stretchid forth, and thou schalt profesie ayens it.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 Lo! Y haue cumpassid thee with boondis, and thou schalt not turne thee fro thi side in `to other side, tille thou fille the daies of thi bisegyng.
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 And take thou to thee wheete, and barli, and beenys, and tillis, and mylie, and vetchis; and thou schalt putte tho in to o vesselle. And thou schalt make to thee looues for the noumbre of daies, bi whiche thou schalt slepe on thi side; bi three hundrid and nynti daies thou schalt ete it.
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 Forsothe thi mete, which thou schalt ete, schal be in weiyte twenti staters in a dai; fro tyme til to tyme thou schalt ete it.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 And thou schalt drynke watir in mesure, the sixte part of hyn; fro tyme til to tyme thou schalt drynke it.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 And thou schalt ete it as barli breed bakun vndur the aischis; and with `a toord that goith out of a man thou schalt hile, it bifore the iyen of hem.
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 The Lord seith these thingis, So the sones of Israel schulen ete her breed defoulid among hethene men, to whiche Y schal caste hem out.
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 And Y seide, A! A! A! Lord God, lo! my soule is not defoulid, and fro my yong childhed til to now Y eet not a thing deed bi it silf, and to-rent of beestis; and al vnclene fleisch entride not in to my mouth.
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 And he seide to me, Lo! Y haue youe to thee the dung of oxis for mennus toordis; and thou schalt make thi breed with it.
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 And he seide to me, Sone of man, lo! Y schal al to-breke the staf of breed in Jerusalem, and thei schulen ete her breed in weiyte and in bisynesse, and thei schulen drynke water in mesure and in angwisch;
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 that whanne breed and watir failen, eche man falle doun to his brother, and thei faile in her wickidnessis.
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

< Ezekiel 4 >