< Ezekiel 24 >

1 And the word of the Lord was maad to me, in the nynthe yeer, and in the tenthe monethe, in the tenthe dai of the monethe,
Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 and he seide, Thou, sone of man, write to thee the name of this dai, in which the king of Babiloyne is confermed ayens Jerusalem to dai.
“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino.
3 And thou schalt seie bi a prouerbe a parable to the hous, terrere to wraththe, and thou schalt speke to hem, The Lord God seith these thingis, Sette thou a brasun pot, sette thou sotheli, and putte thou watir in to it. Take thou a beeste ful fat;
Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti, “‘Ikani mʼphika pa moto, ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.
4 gadere thou togidere the gobetis therof in it, ech good part, and the hipe, and the schuldre, chosun thingis and ful of boonys.
Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama, nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba. Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.
5 Also dresse thou heepis of boonys vndur it; and the sething therof buylide out, and the boonys therof weren sodun in the myddis therof.
Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri. Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo. Madzi awire. Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’
6 Therfor the Lord God seith these thingis, Wo to the citee of bloodis, to the pot whos rust is ther ynne, and the rust therof yede not out of it; caste thou out it bi partis, and bi hise partis; lot felle not on it.
“‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti, “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi, tsoka kwa mʼphika wadzimbiri; dzimbiri lake losachoka! Mutulutsemo nthuli imodzimodzi osasankhulapo.
7 For whi the blood therof is in the myddis therof; he schede it out on a ful cleer stoon, he schedde not it out on erthe,
“‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo. Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala. Sanawakhutulire pa dothi kuopa kuti fumbi lingawafotsere.
8 that it mai be hilid with dust, that Y schulde bringe in myn indignacioun, and `a venge bi veniaunce; Y yaf the blood therof on a ful cleer stoon, that it schulde not be hilid.
Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala kuti asafotseredwe ndi fumbi chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.
9 Therfor the Lord God seith these thingis, Wo to the citee of bloodis, whos brennyng Y schal make greet;
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi! Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.
10 gadere thou togidire boonys, whiche Y schal kyndle with fier; fleischis schulen be wastid, and al the settyng togidere schal be sodun, and boonys schulen faile.
Choncho wonjeza nkhuni ndipo muyatse moto. Phikani nyamayo bwinobwino, muthiremo zokometsera, mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.
11 Also sette thou it voide on coolis, that the metal therof wexe hoot, and be meltid, and that the filthe therof be wellid togidere in the myddis therof, and the rust therof be wastid.
Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo mpaka utenthe kuchita kuti psuu kuti zonyansa zake zisungunuke ndi kuti dzimbiri lake lichoke.
12 It was swat bi myche trauel, and the ouer greet rust therof yede not out therof, nether bi fier.
Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa. Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka ngakhale ndi moto womwe.
13 Thin vnclennesse is abhomynable, for Y wolde clense thee, and thou art not clensid fro thi filthis; but nether thou schalt be clensid bifore, til Y make myn indignacioun to reste in thee.
“‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.
14 Y the Lord spak; it schal come, and Y schal make, Y schal not passe, nethir Y schal spare, nether Y schal be plesid; bi thi weies and bi thi fyndyngis Y schal deme thee, seith the Lord.
“‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’”
15 And the word of the Lord was maad to me,
Yehova anandiyankhula kuti:
16 and he seide, Thou, sone of man, lo! Y take awei fro thee the desirable thing of thin iyen in veniaunce, and thou schalt not weile, nether wepe, nether thi teeris schulen flete doun.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi.
17 Weile thou beynge stille, thou schalt not make mourenyng of deed men; thi coroun be boundun aboute thin heed, and thi schoon schulen be in the feet, nether thou schalt hile the mouth with a cloth, nether thou schalt ete the metis of mourneris.
Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”
18 Therfor Y spak to the puple in the morewtid, and my wijf was deed in the euentid; and Y dide in the morewtid, as he hadde comaundid to me.
Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.
19 And the puple seide to me, Whi schewist thou not to vs what these thingis signefien, whiche thou doist?
Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”
20 And Y seide to hem, The word of the Lord was maad to me,
Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti,
21 and he seide, Speke thou to the hous of Israel, The Lord God seith these thingis, Lo! Y schal defoule my seyntuarie, the pride of youre empire, and the desirable thing of youre iyen, and on which youre soule dredith; and youre sones and youre douytris, whiche ye leften, schulen falle bi swerd.
‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
22 And ye schulen do, as Y dide; ye schulen not hile mouthis with cloth, and ye schulen not ete the mete of weileris.
Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa.
23 Ye schulen haue corouns in youre heedis, and schoon in the feet; ye schulen not weile, nether ye schulen wepe, but ye schulen faile in wretchidnesse, for youre wickidnessis; and ech man schal weile to his brother.
Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu.
24 And Ezechiel schal be to you in to a signe of thing to comynge; bi alle thingis whiche he dide, ye schulen do, whanne this thing schal come; and ye schulen wite, that Y am the Lord God.
Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’
25 And thou, sone of man, lo! in the dai in which Y schal take awei fro hem the strengthe of hem, and the ioie of dignyte, and the desire of her iyen, on whiche the soulis of hem resten, caste awei the sones and douytris of hem;
“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi.
26 in that dai whanne a man fleynge schal come to thee, to telle to thee;
Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo.
27 in that dai sotheli thou schalt opene thi mouth with hym that fledde; and thou schalt speke, and schalt no more be stille; and thou schalt be to hem in to a signe of thing to comynge, and ye schulen witen, that Y am the Lord.
Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 24 >