< Ezekiel 12 >

1 And the word of the Lord was maad to me,
Yehova anayankhula nane kuti,
2 and he seide, Sone of man, thou dwellist in the myddis of an hous terrynge to wraththe, which han iyen to se, and seen not, and eeris to here, and heren not; for it is an hous terrynge to wraththe.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Therfor thou, sone of man, make to thee vessels of passing ouer, and thou schalt passe ouer bi dai bifor hem; forsothe thou schalt passe ouer fro thi place to another place, in the siyt of hem, if perauenture thei biholden, for it is an hous terrynge to wraththe.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 And thou schalt bere withoutforth thi vessels, as the vessels of a man passynge ouer bi dai, in the siyt of hem; sotheli thou schalt go out in the euentid bifore hem, as a man passynge forth goith out.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Bifore the iyen of hem digge the wal to thee, and thou
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 schalt go out thorouy it in the siyt of hem. Thou schalt be borun on schuldris, thou schalt be borun out in derknesse; thou schalt hile thi face, and thou schalt not se the erthe, for Y haue youe thee a signe
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 of thing to comynge to the hous of Israel. Therfor Y dide as the Lord comaundide to me; Y brouyte forth my vessels, as the vessels of a man passynge ouer bi dai, and in the euentid Y diggide a wal to me with hond; Y yede out in derknesse, and Y was borun on schuldris,
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 in the siyt of hem. And the word of the Lord was maad eerli to me,
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 and he seide, Sone of man, whether the hous of Israel, the hous terrynge to wraththe, seiden not to thee, What doist thou?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Seie thou to hem, The Lord God seith these thingis, This birthun is on the duyk, which is in Jerusalem, and on al the hous of Israel, which is in the myddis of hem.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Seie thou, Y am youre signe of thing to comynge; as Y dide, so it schal be don to hem; thei schulen go in to passynge ouer, and in to caitifte.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 And the duyk which is in the myddis of hem, schal be borun out on schuldris, and he schal go out in derknesse; thei schulen digge the wal, and lede hym out; his face schal be hilid, that he se not with iye the erthe.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 And Y schal stretche forth my net on hym, and he schal be takun in my net; and Y schal lede hym in to Babiloyne, in to the lond of Caldeis, and he schal not se that lond, and he schal die there.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 And Y schal scatere in to ech wynd alle men that ben aboute hym, his help, and hise cumpenyes; and Y schal draw out the swerd aftir hem.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 And thei schulen wite, that Y am the Lord, whanne Y schal scatere hem among hethene men, and schal sowe hem abrood in londis.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 And Y schal leue of hem a fewe men fro swerd, and hungur, and pestilence, that thei telle out alle the grete trespassis of hem among hethene men, to which thei schulen entre; and thei schulen wite, that Y am the Lord.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 And the word of the Lord was maad to me,
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 and he seide, Thou, sone of man, ete thi breed in disturblyng, but also drynke thi water in haaste and mourening.
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 And thou schalt seie to the puple of the lond, The Lord God seith these thingis to hem that dwellen in Jerusalem, in the lond of Israel, Thei schulen ete her breed in angwisch, and thei schulen drynke her watir in desolacioun; that the lond be desolat of his multitude, for the wickidnesse of alle men that dwellen ther ynne.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 And citees that ben now enhabitid, shulen be desolat, and the lond schal be forsakun; and ye schulen wite, that Y am the Lord.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 And the word of the Lord was maad to me,
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 and he seide, Sone of man, what is this prouerbe to you, of men seiynge in the lond of Israel, Daies schulen be differrid in to long tyme, and ech visioun shal perische?
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 Therfor seie thou to hem, The Lord God seith these thingis, Y schal make this prouerbe to ceesse, and it schal no more be seid comynli in Israel; and speke thou to hem, that the daies han neiyid, and ech word of profesie.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 For whi ech visioun schal no more be voide, nether bifor tellyng of thing to comynge schal be douteful in the myddis of the sones of Israel;
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 for Y the Lord schal speke what euer word Y schal speke, and it schal be don; it schal no more be delaied, but in youre daies, ye hous terrynge to wraththe, Y schal speke a word, and Y schal do that word, seith the Lord God.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 And the word of the Lord was maad to me, and he seide, Thou,
Yehova anandiyankhula nati:
27 sone of man, lo! the hous of Israel, of hem that seien, The visioun which this man seeth, is in to manye daies, and this man profesieth in to longe tymes.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 Therfor seie thou to hem, The Lord God seith these thingis, Ech word of me schal no more be deferrid; the word which Y schal speke, schal be fillid, seith the Lord God.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”

< Ezekiel 12 >