< Exodus 7 >

1 And the Lord seide to Moises, Lo! Y haue maad thee the god of Farao; and Aaron, thi brother, schal be thi prophete.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
2 Thou schalt speke to Aaron alle thingis whiche Y comaunde to thee, and he schal speke to Farao, that he delyuere the sones of Israel fro his hond.
Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
3 But Y schal make hard his herte, and Y schal multiplie my signes and merueils in the lond of Egipt, and he schal not here you;
Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
4 and Y schal sende myn hond on Egipt, and Y schal lede out myn oost, and my puple, the sones of Israel, fro the lond of Egipt bi mooste domes;
iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
5 and Egipcians schulen wite, that Y am the Lord, which haue holde forth myn hond on Egipt, and haue led out of the myddis of hem the sones of Israel.
Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
6 And so Moises dide and Aaron; as the Lord comaundide, so thei diden.
Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
7 Forsothe Moyses was of fourescoor yeer, and Aaron was of fourescoor yeer and thre, whanne thei spaken to Farao.
Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
8 And the Lord seide to Moises and to Aaron,
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
9 Whanne Farao schal seie to you, Schewe ye signes to vs, thou schalt seie to Aaron, Take thi yerde, and caste forth it before Farao, and be it turned into a serpent.
“Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
10 And so Moises and Aaron entriden to Farao, and diden as the Lord comaundide; and Aaron took the yeerde, and castide forth bifore Farao and hise seruauntis, which yerde was turned in to a serpent.
Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
11 Forsothe Farao clepide wise men, and witchis, and thei also diden bi enchauntementis of Egipt, and bi summe priuy thingis in lijk maner;
Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
12 and alle castiden forth her yerdis, whiche weren turned in to dragouns; but the yerde of Aaron deuouride `the yerdis of hem.
Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
13 And the herte of Farao was maad hard, and he herde not hem, as the Lord comaundide.
Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
14 Forsothe the Lord seide to Moyses, The herte of Farao is maad greuouse, he nyle delyuere the puple;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
15 go thou to hym eerli; lo! he schal go out to the watris, and thou schalt stonde in the comyng of hym on the brynke of the flood; and thou schalt take in thin honde the yerde, that was turned into a dragoun,
Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
16 and thou schalt seie to hym, The Lord God of Ebrews sente me to thee, and seide, Delyuere thou my puple, that it make sacrifice to me in desert; til to present time thou noldist here.
Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
17 Therfor the Lord seith these thingis, In this thou schalt wite, that Y am the Lord; lo! Y schal smyte with the yerde, which is in myn hond, the watir of the flood, and it schal be turned in to blood;
Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
18 and the fischis that ben in the flood schulen die; and the watris schulen wexe rotun, and Egipcians drynkynge the watir of the flood schulen be turmentid.
Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
19 Also the Lord seide to Moises, Seie thou to Aaron, Take thi yerde, and holde forth thin hond on the watris of Egipt, and on the flodis of hem, and on the stremys `of hem, and on the mareis, and alle lakis of watris, that tho be turned in to blood; and blood be in al the lond of Egipt, as wel in vessils of tree as of stoon.
Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
20 And Moises and Aaron diden so, as the Lord comaundide; and Aaron reiside the yerde, and smoot the watir of the flood bifore Farao and hise seruauntis, which watir was turned in to blood;
Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
21 and fischis, that weren in the flood, dieden; and the flood was rotun, and Egipcians myyten not drynke the water of the flood; and blood was in al the lond of Egipt.
Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
22 And the witchis of Egipcians diden in lijk maner by her enchauntementis; and the herte of Farao was maad hard, and he herde not hem, as the Lord comaundide.
Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
23 And he turnede awei hym silf, and entride in to his hows, nethir he took it to herte, yhe, in this tyme.
Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
24 Forsothe alle Egipcians diggiden watir `bi the cumpas of the flood, to drinke; for thei myyten not drynke of the `watir of the flood.
Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
25 And seuene daies weren fillid, aftir that the Lord smoot the flood.
Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.

< Exodus 7 >