< Exodus 12 >

1 Also the Lord seide to Moises and Aaron in the lond of Egipt,
Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
2 This monethe, the bigynnyng of monethis to you, schal be the firste in the monethis of the yeer.
“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
3 Speke ye to al the cumpanye of the sones of Israel, and seie ye to hem, In the tenthe dai of this monethe ech man take a lomb by hise meynees and housis;
Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
4 but if the noumbre is lesse, that it may not suffice to ete the lomb, he schal take his neiybore, which is ioyned to his hows, bi the noumbre of soulis, that moun suffice to the etyng of the lomb.
Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
5 Forsothe the lomb schal be a male of o yeer, without wem; bi which custom ye schulen take also a kide;
Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
6 and ye schulen kepe hym til to the fouretenthe dai of this monethe; and al the multitude of the sones of Israel schal offre hym at euentid.
Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
7 And thei schulen take of his blood, and schulen put on euer either post, and in lyntels, `ether hiyer threschfoldis, of the housis, in whiche thei schulen ete hym;
Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
8 and in that niyt thei schulen ete fleischis, roostid with fier, and therf looues, with letusis of the feeld.
Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
9 Ye schulen not ete therof ony raw thing, nether sodun in watir, but roostid oneli by fier; ye schulen deuoure the heed with feet and entrailis therof;
Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
10 nether ony thing therof schal abide til the morewtid; if ony thing is residue, ye schulen brenne in the fier.
Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
11 Forsothe thus ye schulen ete hym; ye schulen girde youre reynes, and ye schulen haue schoon in the feet, and ye schulen holde stauys in hondis, and ye schulen ete hastili; for it is fase, that is, the passyng of the Lord.
Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
12 And Y schal passe thorou the lond of Egipt in that niyt, and Y schal smyte al the firste gendrid thing in the lond of Egipt, fro man til to beeste; and Y the Lord schal make domes in alle the goddis of Egipt.
“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
13 Forsothe blood schal be to you in to signe, in the housis in whiche ye schulen be; and Y schal se the blood, and Y schal passe you; nether a wounde distriynge schal be in you, whanne Y schal smyte the lond of Egipt.
Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
14 Forsothe ye schulen haue this dai in to mynde, and `ye schulen make it solempne to the Lord in youre generaciouns bi euerlastynge worschipyng.
“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
15 In seuene daies ye schulen ete therf breed; in the firste dai no thing diyt with sour douy schal be in youre housis; who euer schal ete ony thing diyt with sour douy, fro the firste dai til the seuenthe dai, that soule schal perische fro Israel.
Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
16 The firste day schal be hooli and solempne, and the seuenthe dai schal be worschipful bi the same halewyng; ye schulen not do ony werk in tho daies, outakun these thingis that perteynen to mete;
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
17 and ye schulen kepe therf breed. For in that same dai Y schal lede out of the lond of Egipt youre oost; and ye schulen kepe this dai in youre generaciouns bi euerlastynge custom.
“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
18 In the first monethe, in the fouretenthe dai of the monethe, at euentid, ye schulen ete therf breed, til to the oon and twentithe dai of the same monethe at euentid.
Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
19 In seuene dayes no thing `diyt with sour douy schal be foundun in youre housis; if ony etith ony thing diyt with sour dow, his soule schal perische fro the cumpeny of Israel, as wel of comelyngis, as of hem that ben borun in the lond.
Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
20 Ye schulen not ete ony thing diyt with sour dow, and ye schulen ete therf breed in alle youre dwellyng placis.
Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
21 Forsothe Moises clepide alle the eldre men of the sones of Israel, and seide to hem, Go ye, and take a beeste by youre meynees, and offre ye fase; and dippe ye a bundel of isope,
Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
22 in the blood which `is in the threisfold, and sprynge ye therof the lyntel, and euer either post; noon of you schal go out at the dore of his hows til the morewtid.
Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
23 For the Lord schal passe smytynge Egipcians; and whanne he schal se the blood in the lyntel, and in euer either post, he schal passe the dore of the hows; and he schal not suffre the smytere to entre in to youre housis, and to hirte.
Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
24 Kepe thou this word; it schal be a lawful thing to thee and to thi sones til in to with outen ende.
“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
25 And whanne ye schulen entre in to the lond which the Lord schal yyue to you, as he bihiyte, ye schulen kepe these cerymonyes;
Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
26 and whanne youre sones schulen seie to you, What is this religioun? ye schulen seie to hem,
Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
27 It is the sacrifice of the passyng of the Lord, whanne he passide ouer the housis of the sones of Israel in Egipt, and smoot Egipcians, and delyueride oure housis. And the puple was bowid, and worschipide.
Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
28 And the sones of Israel yeden out, and diden as the Lord comaundide to Moises and to Aaron.
Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
29 Forsothe it was doon in the myddis of the nyyt, the Lord smoot al the firste gendrid thing in the lond of Egipt, fro the firste gendrid of Farao, that sat in the trone of hym, til to the first gendrid of the caitif womman, that was in the prisoun, and alle the first gendrid of beestis.
Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
30 And Farao roos in the nyyt, and alle hise seruauntis, and al Egipt; and a greet cry was maad in Egipt, for noon hows was, in which a deed man lay not.
Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
31 And whanne Moises and Aaron weren clepid in the nyyt, Farao seide, Rise ye, go ye out fro my puple, bothe ye and the sones of Israel; go ye, offre ye to the Lord, as ye seien;
Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
32 take ye youre scheep and greete beestis, as ye axiden; and go ye, and blesse ye me.
Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
33 And Egipcians constreyneden the puple to go out of the lond swiftli, and seiden, All we schulen die!
Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
34 Therfor the puple took meele spreynd togidere, bifor that it was diyt with sour douy; and boond in mentils, and puttide on her schuldris.
Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
35 And the sones of Israel diden as the Lord comaundide to Moises; and thei axiden of Egipcians siluerne vesselis and goldun, and ful myche clooth.
Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
36 Forsothe the Lord yaf grace to the puple bifor Egipcians, that the Egipcians lenten to hem; and thei maden bare Egipcians.
Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
37 And the sones of Israel yeden forth fro Ramasses in to Socoth, almest sixe hundrid thousind of foot men, with out litle children and wymmen;
Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
38 but also comyn puple of malis and femalis vnnoumbrable stieden with hem; scheep, and oxun, and ful many beestis of diuerse kynde, stieden with hem.
Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
39 And thei bakiden meele, which spreynd to gidere `a while ago thei token fro Egipt, and maden therf looues bakun vnder the aischis; for the looues miyten not be diyt with sour dow, for Egipcians compelliden to go out, and suffriden not to make ony tariyng, nether it was leiser to make ony seew.
Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
40 Forsothe the dwellyng of the sones of Israel, bi which thei dwelliden in Egipt, was of foure hundrid and thretti yeer;
Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
41 and whanne tho weren fillid, al the oost of the Lord yede out of the lond of Egipt in the same dai.
Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
42 This nyyt is worthi to be kept in the worschipyng of the Lord, whanne he ladde hem out of the lond of Egipt; alle the sones of Israel owen to kepe this in her generaciouns.
Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
43 Also the Lord seide to Moises and Aaron, This is the religioun of fase; ech alien schal not ete therof;
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
44 sotheli ech seruaunt bouyt schal be circumcidid, and so he schal ete;
Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
45 a comelyng and hirid man schulen not ete therof;
Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
46 it schal be etun in oon hows; nether ye schulen bere out of the fleischis therof; nether ye schulen breke a boon therof.
“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
47 Ech company of the sones of Israel schal make that fase;
Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
48 that if ony pilgrym wole passe into youre feith and worschipyng, and make fase of the Lord, ech male kynde of hym schal be circumcidid bifore, and thanne he schal make lawfuli, and he schal be to gidere as a man borun of the lond; forsothe if ony man is not circumcidid, he schal not ete therof.
“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
49 The same lawe schal be to a man borun of the lond, and to a comelyng, that takith youre feith, which is a pilgrym anentis you.
Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
50 And alle the sones of Israel diden as the Lord comaundide to Moises and Aaron.
“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
51 And in the same dai the Lord ladde out of `the lond of Egipt the sones of Israel, bi her cumpanies.
Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”

< Exodus 12 >